Zilengezo
◼ Cogaŵila ca mu September ndi October: Magazini a Nsanja ya Mlonda ndi Galamukani! November ndi December: Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni kapena Kodi Mufuna Kudziŵa Mayankho Azoona pa Mafunso Aya?
◼ Nkhani yapadela ya panyengo ya Cikumbutso ca 2014 idzakambidwa mlungu wa April 21. Mutu wa nkhaniyi udzalengezedwa m’tsogolo. Mipingo imene idzakhale ndi woyang’anila dela kapena msonkhano wadela mlungu umenewo idzakhale ndi nkhaniyi mlungu wotsatila. Mpingo uliwonse usadzakhale ndi nkhaniyi pasanafike pa April 21.
◼ Kuyambila ndi magazini a September 2013, Galamukani! iziikidwa m’kati mwa Nsanja ya Olonda yogaŵila. Pakali pano, mipingo imalandila magazini aŵili a Galamukani! kapena a Nsanja ya Olonda ophatikizidwa pamodzi. Mgwilizanitsi wa Bungwe la Akulu ayenela kukonza cilengezo cofotokoza njila yatsopano yolandilila magazini imeneyi cimene cidzapelekedwa pa Msonkhano wa Nchito. Cilengezo cimeneci ciyenela kupelekedwa pamene kwatsala nthawi yocepa kuti muike magazini a September pa malo amene ofalitsa amatengela magazini ao oŵelenga. M’bale amene akulengeza ayenela kuonetsa ofalitsa mmene magazini angagaŵilidwile mu ulaliki. Ngati mudzakhala mutalandila magaziniwa, mungacotseletu Galamukani m’kati mwa Nsanja ya Olonda, kapena mungaisolole pang’ono kuti mwini nyumba aone kuti akulandila Nsanja ya Olonda ndi Galamukani!
◼ Zofalitsa Zatsopano Zimene Zilipo:
“Khalanibe M’cikondi ca Mulungu”—Cinyanja
Uthenga Wabwino Wocokela Kwa Mulungu—Nsenga