LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 10/14 tsa. 3
  • Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
km 10/14 tsa. 3

Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki

Tidzakambilana mafunso otsatilawa pa Sukulu ya Ulaliki mkati mwa mlungu wa October 27, 2014.

  1. Malinga ndi Numeri 21:5, n’cifukwa ciani Aisiraeli anali kuŵilingula kwa Mulungu ndi kwa Mose? Ndi cenjezo lotani limene tipezapo? [Sept. 1, w99 8/15 mas. 26-27]

  2. N’cifukwa ciani Yehova anakwiyila Balamu? (Num. 22:20-22) [Sept. 8, w04 8/1 tsa. 27 ndime 2]

  3. 3. Kodi lemba la Numeri 25:11 litiuza ciani za khalidwe la Pinihasi? Nanga tingatengele bwanji citsanzo cake? [Sept. 8, w04 8/1 tsa. 27 ndime 4]

  4. Ndi m’njila ziti zimene Mose anationetsela citsanzo cabwino kwambili ca kudzicepetsa? (Num. 27:5, 15-18) [Sept. 15, w13 2/1 tsa. 5]

  5. Kodi Yoswa ndi Kalebe anapelekela bwanji umboni wamphamvu woonetsa kuti anthu opanda ungwilo akhoza kuyenda m’njila za Mulungu ngakhale akumane ndi citsutso? (Num. 32:12) [Sept. 22, w93 11/15 tsa. 14 ndime 13]

  6. Kodi kumvela kwa ana aakazi a Tselofekadi kukukhudza bwanji mmene Akristu osakwatila kapena osakwatiwa amaonela cikwati? (Num. 36:10-12) [Sept. 29, w08 2/15 mas. 4-5 ndime 10]

  7. Kodi kudandaula ndi kulankhula mau oipa kunawabweletsela vuto lanji Aisiraeli, ndipo ife tiphunzilapo ciani pankhani imeneyi? (Deut. 1:26-28, 34, 35) [Oct. 6, w13 8/15 tsa. 11 ndime 7]

  8. Pofuna kuti Aisiraeli adalitsidwe ndi kuti akhale ndi moyo wabwino m’Dziko Lolonjezedwa, kodi Yehova anawapatsa maudindo aŵili ati? (Deut. 4:9) [Oct. 13, w06 6/1 tsa. 29 ndime 15]

  9. Kodi zinatheka bwanji kuti zovala za Aisiraeli zisathe ndiponso kuti mapazi ao asatupe paulendo wa m’chipululu? (Deut. 8:3, 4) [Oct. 20, w04 9/15 tsa. 26 ndime 1]

  10. Tingagwilitsile nchito motani cilimbikitso cimene Aisiraeli anapatsidwa cakuti “amamatile” kwa Yehova? (Deut. 13:4, 6-9) [Oct. 27, w02 10/15 tsa. 16 ndime 14]

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani