LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 January tsa. 6
  • “Padziko Lonse Lapansi Panali Cilankhulo Cimodzi”

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • “Padziko Lonse Lapansi Panali Cilankhulo Cimodzi”
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 January tsa. 6
Anthu amene anali kumanga nsanja ya Babele analephela kumvelana Yehova atasokoneza cinenelo cawo.

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | GENESIS 9-11

“Padziko Lonse Lapansi Panali Cilankhulo Cimodzi”

11:1-4, 6-9

Pa Babele, Yehova anabalalitsa anthu osamvela mwa kusokoneza citundu cawo. Masiku ano, iye akusonkhanitsa khamu lalikulu kucokela m’maiko onse na m’zinenelo, ndipo akuwapatsa “cilankhulo coyela” kuti “aziitanila pa dzina la Yehova na kumutumikila mogwilizana.” (Zef. 3:9; Chiv. 7:9) “Cilankhulo coyela” cimeneci ni coonadi conena za Yehova komanso zolinga zake zopezeka m’Malemba.

Kuphunzila citundu catsopano kumafuna zambili kuposa cabe kudziŵa mawu atsopano. Kumafuna kuphunzila kaganizidwe katsopano. Mofananamo, pamene tiphunzila cilankhulo coyela ca coonadi, maganizo athu amasintha. (Aroma 12:2) Kusintha kumeneku kumapitiliza, ndipo kumathandiza anthu a Mulungu kukhala ogwilizana. —1 Akor. 1:10.

Abale na alongo akuceza mosangalala misonkhano isanayambe.
    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani