LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 May tsa. 7
  • Yesani Kudziŵa Cithunzi ca Nkhani Yonse

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Yesani Kudziŵa Cithunzi ca Nkhani Yonse
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Nkhani Zofanana
  • Abale Ake Amuzonda Yosefe
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • ‘Tamvelani Maloto Awa’
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Yehova Sanamuiŵale Yosefe
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Kapolo Amene Anamvela Mulungu
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 May tsa. 7
Zithunzi: M’bale wacicepele aganizila zimene aŵelenga m’Baibo zokhudza Yosefe. 1. Yosefe agwela m’citsime copanda madzi. 2. Yosefe akuyenda pamodzi na gulu lapaulendo la Amidiyani limene likupita ku Iguputo. 3. Mkazi wa Potifara akuyang’ana Yosefe ca patali pamene Yosefeyo akamba na mwamuna wake.

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Yesani Kudziŵa Cithunzi ca Nkhani Yonse

Poŵelenga nkhani za m’Baibo, yesani kudziŵa cithunzi ca nkhani yonse. Ŵelengani malemba ena ozungulila, phunzilani za anthu a m’nkhaniyo, komanso zifukwa zimene zinapangitsa kuti acite zinthu zimene anacitazo. M’maganizo mwanu, onani zinthuzo, mvelani mawuwo, nunkhizani tumafungo tokomato, ndiponso mvelani mmene anthu a m’nkhaniyo anali kumvelela.

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI MMENE TINGAPINDULILE KWAMBILI POŴELENGA BAIBO—KAMBALI KAKE, PAMBUYO PAKE YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:

  • Yosefe asanagulitsidwe ku ukapolo.

    Kodi n’zifukwa ziti zimene mwina zinapangitsa kuti abale ake a Yosefe asamagwilizane naye?

  • Yosefe akuyenda pamodzi na gulu lapaulendo la Amidiyani limene likupita ku Iguputo.

    N’ciani cimene mwina cinapangitsa abale ake a Yosefe nthawi zina kumacita zinthu mwaukali popanda kuganizila zotulukapo zake?

  • Zithunzi: Yakobo acitapo kanthu kuti athetse kusemphana maganizo na Esau. 1. Yakobo apemphela. 2. Yakobo agwada pamaso pa Esau. 3. Esau akumbatila Yakobo.

    Tingaphunzile ciani m’Malemba zokhudza Yakobo, tate wake wa Yosefe?

  • Kodi Yakobo anawaphunzitsa mfundo yabwino iti ana ake pankhani yothetsa kusemphana maganizo?

  • Kodi mwapindula bwanji na vidiyoyi?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani