LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp23 na. 1 tsa. 5
  • Mulungu Amasamala za Inu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mulungu Amasamala za Inu
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2023
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Baibo Inganithandize Ngati Nili na Maganizo Ofuna Kudzipha?
    Kuyankha Mafunso Okhudza Baibo
  • Mulungu Walonjeza Kuti Matenda a Maganizo Adzathelatu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2023
  • Matenda a Maganizo ni Mlili wa Padziko Lonse
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2023
  • 2 | “Malemba . . . Amatilimbikitsa”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2023
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2023
wp23 na. 1 tsa. 5
Mnyamata wakhala pansi pafupi na bedi lake ndipo akuŵelenga Baibo.

Mulungu Amasamala za Inu

M’Baibo muli malangizo abwino kwambili cifukwa ni buku locokela kwa Mulungu. Baibo si buku la malangizo a zaumoyo. Komabe, ingatithandize kudziŵa zimene tingacite tikakumana na zinthu zosoŵetsa mtendele, tikamavutika maganizo, tikapwetekedwa mtima, kapena tikadwala matenda odetsa nkhawa.

Koposa zonse, Baibo imatitsimikizila kuti Mlengi wathu, Yehova Mulungu,a amamvetsa maganizo athu na mmene timamvela kuposa munthu wina aliyense. Iye ni wofunitsitsa kutithandiza pa mavuto aliwonse amene timakumana nawo. Mwacitsanzo, onani malemba aŵili awa olimbikitsa:

“Yehova ali pafupi ndi anthu a mtima wosweka. Ndipo odzimvela cisoni mumtima mwawo amawapulumutsa.”—SALIMO 34:18.

“Pakuti ine, Yehova Mulungu wako, ­ndagwila dzanja lako lamanja. Ine amene ndikukuuza kuti, ‘Usacite mantha. Ineyo ndikuthandiza.’”—YESAYA 41:13.

Koma kodi Yehova amatithandiza bwanji ngati tikudwala matenda a maganizo? Monga muonele m’nkhani zotsatilazi, Yehova amatithandiza m’njila zambili poonetsa kuti amasamaladi za ife.

a Yehova ni dzina la Mulungu.—Salimo 83:18.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani