LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • g19 na. 3 tsa. 3
  • Buku Lakale-kale, Koma Lothandiza Masiku Ano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Buku Lakale-kale, Koma Lothandiza Masiku Ano
  • Galamuka!—2019
  • Nkhani Zofanana
  • Za m’Kope Ino ya Galamuka!: Kodi Baibo Ingakuthandizeni Kukhala na Umoyo Wabwino?
    Galamuka!—2019
  • Zamkati
    Galamuka!—2019
  • 4 | Baibo Ili na Malangizo Othandiza
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2023
  • N’zotheka Kukhala Na Umoyo Wacimwemwe Pali Pano
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2019
Onaninso Zina
Galamuka!—2019
g19 na. 3 tsa. 3
Ayang’ana Mabaibo akale m’miziyamu

Buku Lakale-kale, Koma Lothandiza Masiku Ano

Anthu ambili amaona kuti Baibo ni buku lopatulika. N’zoona kuti Baibo ni buku lopatulika limene limatiuza mmene tingalambilile Mulungu. Koma lilinso na malangizo othandiza mu umoyo wathu wa tsiku na tsiku.

Mwacitsanzo, onani zimene ena anakamba zoonetsa mmene anapindulila cifukwa coŵelenga Baibo, na kuseŵenzetsa malangizo ake.

“Umoyo wanga uli bwino tsopano. Maganizo na mtima wanga zili m’malo. Lomba nili na umoyo wacimwemwe kwambili.”—Fiona.

“Mwa kuŵelenga Baibo, moyo wanga wakhala wopindulitsa komanso wa colinga.”—Gnitko.

“Umoyo wanga wasintha kwambili kukhala wabwino. Manje nili na umoyo wosalila zambili, ndipo nimapeza nthawi yokwanila yoceza na banja langa.”—Andrew.

Palinso zitsanzo zina zambili monga zimenezi. Zungulile dziko lonse, ambili apeza kuti Baibo imapeleka malangizo othandiza mu umoyo wa tsiku na tsiku.

Tiyeni tione mmene Baibo ingathandizile anthu m’mbali zotsatilazi:

  • Thanzi labwino

  • Kudziŵa kulamulila mtima wathu

  • Umoyo wa banja komanso mabwenzi

  • Moseŵenzetsela ndalama

  • Umoyo wauzimu

Baibo ni buku locokela kwa Mulungu, ndipo ingakuthandizeni mu umoyo wanu wa tsiku na tsiku.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani