LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • my nkhani 99
  • M’cipinda Capamwamba

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • M’cipinda Capamwamba
  • Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Mgonelo wa Ambuye
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Mgonelo wa Ambuye—Mwambo Umene Umalemekeza Mulungu
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Zimene Mwambo Wosalila Zambili Umatiphunzitsa Ponena za Mfumu Yathu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2019
  • ‘Ici Cidzakhala Cikumbutso Kwa Inu’
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
my nkhani 99

Nkhani 99

M’cipinda Capamwamba

MASIKU aŵili apitapo, tsopano n’pa Cinai nthawi yausiku. Yesu ndi atumwi ake 12 abwela m’cipinda capamwamba ici kuti acite Paska. Mwamuna amene acoka uyo ni Yudasi Isikariyoti. Apa m’pamene ayenda kukauza ansembe mmene angagwilile Yesu.

Kutatsala tsiku limodzi kuti acite Paska, Yudasi anayenda kwa io kukawafunsa kuti: ‘Kodi mudzanipatsa ciani nikakuthandizani kugwila Yesu?’ Iwo anati: ‘Ndalama 30 zasiliva.’ Conco Yudasi tsopano ayenda kukumana ndi amuna amenewa kuti awapeleke kumene kuli Yesu. Cimeneci ni cinthu coipa kwambili, si conco?

Paska yatha, koma Yesu tsopano ayamba phwando lina lapadela. Apeleka mkate kwa atumwi ake ndi kuwauza kuti: ‘Idyani cifukwa mkate uwu uimila thupi langa limene lidzapelekedwa kaamba ka inu.’ Ndiyeno awapatsa kapu ya vinyo ndi kuwauza kuti: ‘Imwani, vinyo ameneyu aimila magazi anga amene adzakhetsedwa kaamba ka inu.’ Baibo imacha phwando limeneli kuti ‘Mgonelo wa Ambuye,’ kapena Cakudya Camadzulo ca Ambuye.’

Aisiraeli anali kucita Paska pokumbukila nthawi imene mngelo wa Mulungu ‘anapitilila’ nyumba zao mu Iguputo, koma anapha ana oyamba mu nyumba za Aiguputo. Koma tsopano Yesu afuna kuti otsatila ake azimukumbukila, komanso kuti azikumbukila mmene anapelekela moyo wake kaamba ka io. Ndipo n’cifukwa cake awauza kuti azicita phwando lapadela limeneli caka ciliconse.

Pamene anatsiliza kucita Mgonelo wa Ambuye, Yesu auza atumwi ake kuti afunika kukhala olimba mtima ndi okhulupilika kwambili. Potsilizila pake, aimba nyimbo zotamanda Mulungu ndi kucoka pamalowo. Tsopano ni nthawi yausiku kwambili, mwinamwake kupitilila pakati pausiku. Tiye tione kumene io ayenda.

Mateyu 26:14-30; Luka 22:1-39; Yohane caputa 13 mpaka 17; 1 Akorinto 11:20.

Mafunso Ophunzilila

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani