LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • gf phunzilo 1 tsa. 3
  • Mulungu Akupemphani Kuti Mukhale Mnzake

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mulungu Akupemphani Kuti Mukhale Mnzake
  • Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Nkhani Zofanana
  • Mukhoza Kukhala Bwenzi la Yehova
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Muganiza Bwanji?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2018
  • Kukhala Bwenzi la Yehova
    ‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
gf phunzilo 1 tsa. 3

Phunzilo 1

Mulungu Akupemphani Kuti Mukhale Mnzake

Mulungu afuna kuti imwe mukhale mnzake. Kodi munaganizapo kuti imwe mungakhale mnzake wa Mulungu? Abulahamu, amene anakhalako kale kwambili, anali mnzake wa Mulungu. (Yakobo 2:23) Baibo imakamba za anthu ena amene anali anzake a Mulungu, ndipo Mulungu anawadalitsa kwambili. Masiku ano, padziko lonse lapansi, pali anthu amene akhala anzake a Mulungu. Na imwe mungakhale mnzake wa Mulungu.

Mulungu angakhale mnzanu woposa mnzanu aliyense. Mulungu salephela kucita zimene amalonjeza kwa anzake okhulupilika. (Salmo 18:25) Kukhala mnzake wa Mulungu nikwabwino kuposa kukhala na cuma. Munthu wolemela akafa, anthu ena amatenga cuma cake. Koma cuma cimene anzake a Mulungu ali naco, palibe munthu amene angacitenge.—Mateyu 6:19.

Anthu ena angayese kukuletsani kuphunzila za Mulungu. Ngakhale anzanu kapena acibanja angafune kukuletsani. (Mateyu 10:36, 37) Ngati ena akusekani kapena kukuopsani, mudzifunse kuti, ‘Kodi ine nifuna kukondweletsa ndani—anthu kapena Mulungu?’ Ganizilani izi: Ngati munthu wina akuuzani kuti muleke kudya, kodi mungaleke? Iyai. Mukaleka kudya mungafe. Koma Mulungu angakupatseni moyo wosatha! Conco, musavomele kuti aliyense akuletseni kuphunzila za kukhala mnzake wa Mulungu.—Yohane 17:3.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani