LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • gf phunzilo 14 masa. 22-23
  • Anzake a Mulungu Amakana Kucita Voipa

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Anzake a Mulungu Amakana Kucita Voipa
  • Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Tiyenela Kucita Ciani Kuti Tikondweletse Mulungu?
    Mvetselani kwa Mulungu Kuti Mukhale ndi Moyo Wamuyaya
  • Gao 13
    Mvetselani kwa Mulungu
  • Muganiza Bwanji?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2018
  • Kukhala ndi Moyo Wokondweletsa Mulungu
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
Onaninso Zina
Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
gf phunzilo 14 masa. 22-23

Phunzilo 14

Anzake a Mulungu Amakana Kucita Voipa

Satana amanyengelela anthu kuti azicita vinthu voipa. Munthu amene amafuna kukhala mnzake wa Mulungu, naye afunika kuzonda vimene Mulungu amazonda. (Salmo 97:10) Onani vinthu vina voipa vimene anzake a Mulungu amakana kucita:

Macimo a zogonana. “Usacite cigololo.” (Eksodo 20:14) Nako kugonana mukalibe kukwatilana ni kulakwa.—1 Akorinto 6:18.

Kuledzela kapena ‘kukolewa.’ “Oledzela, . . . sadzaloŵa Ufumu wa Mulungu.”—1 Akorinto 6:10.

Kupha munthu, Kucotsa mimba. “Usaphe.”—Eksodo 20:13.

Kuba. “Usabe.”—Eksodo 20:15.

Kunama. Yehova amazonda munthu wa “lilime lonama.”—Miyambo 6:17.

Ciwawa na kukalipa kopitilila. ‘Yehova . . . amuda woipa ndi iye wakukonda ciwawa.’ (Salmo 11:5) ‘Nchito za thupi, . . . [ziphatikizapo] kupsa mtima.’—Agalatiya 5:19, 20.

Njuga. “Muleke kuyanjana ndi aliyense . . . waumbombo.”—1 Akorinto 5:11, NW.

Kuzondana cifukwa cosiyana khungu (nkhanda) kapena kusiyana mitundu. ‘Kondanani nao adani anu, ndi kupemphelela iwo akuzunza inu.’—Mateyu 5:43, 44.

Zimene Mulungu amatiuza zimatipindulitsa. Nthawi zina cimavuta kukana voipa. Koma Yehova na Mboni zake angakuthandizeni kukana kucita voipa vimene Mulungu samafuna.—Yesaya 48:17; Afilipi 4:13; Ahebri 10:24, 25.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani