Nyimbo 11
Tikondweretse Mtima wa Yehova
(Miyambo 27:11)
1. M’lungu takulonjezani,
kuchita zofuna zanu.
Tidzagwira ntchito yanu
Mtima wanu ukondwere.
2. Kapolo wanu padziko,
Amapereka chakudya
Iye amatithandiza
Kuchita zofuna zanu.
3. Mutipatse mzimu wanu,
Kuti tikhulupirike
Inde tikutamandeni,
Mtima wanu ukondwere.
(Onaninso Mat. 24:45-47; Luka 11:13; 22:42.)