LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • T-31 masa. 1-4
  • Kodi Zinthu Zidzakhala Bwanji Mtsogolo?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Zinthu Zidzakhala Bwanji Mtsogolo?
  • Kodi Zinthu Zidzakhala Bwanji Mtsogolo?
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Ufumu wa Mulungu Ndi Ciani?
    Kodi Ufumu wa Mulungu Ndi Ciani?
  • Kodi Mavuto Adzathadi?
    Kodi Mavuto Adzathadi?
  • Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli?
    Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli
  • Kodi N’zoona Kuti Akufa Angakhalenso ndi Moyo?
    Kodi N’zoona Kuti Akufa Angakhalenso ndi Moyo?
Onaninso Zina
Kodi Zinthu Zidzakhala Bwanji Mtsogolo?
T-31 masa. 1-4

Kodi Zinthu Zidzakhala Bwanji Mtsogolo?

Kodi dziko lathu . . .

  • lidzakhala mmene lililimu?

  • lidzaipilatu?

  • lidzakhala bwino?

ZIMENE BAIBO IMANENA

“Mulungu. . . adzapukuta misozi yonse m’maso mwao, ndipo imfa sidzakhalaponso. Sipadzakhalanso kulila, kapena kubuula, ngakhale kupweteka. Zakalezo zapita.”—Chivumbulutso 21:3, 4, Baibulo la Dziko Latsopano.

UBWINO WOKHULUPILILA ZIMENEZI

Mudzakhala ndi nchito yabwino ndi yokhutilitsa.—Yesaya 65:21-23.

Simudzadwalanso kapena kuvutika mwa njila iliyonse.—Yesaya 25:8; 33:24.

Mudzakhala ndi moyo wabwino kwamuyaya, inu ndi banja lanu ndi mabwenzi anu.—Salimo 37:11, 29.

Mwamuna ndi mkazi ayang’ana mwacidalilo kutsogolo; kamtsikana kathilila duwa; anchito akumanga nyumba

KODI TINGAKHULUPILILEDI ZIMENE BAIBO IMANENA?

Inde, pa zifukwa ziŵili izi:

  • Mulungu ali ndi mphamvu yokwanilitsa lonjezo limeneli. M’Baibo, ndi Yehova Mulungu yekha amene amachedwa kuti “Wamphamvuyonse,” cifukwa cakuti ali ndi mphamvu zopanda malile. (Chivumbulutso 15:3) Conco, iye sangalephele ngakhale pang’ono kukwanilitsa lonjezo lake lakuti adzasintha dziko lathu kuti likhale labwino, pakuti Baibo imanena kuti “zinthu zonse n’zotheka kwa Mulungu.”—Mateyu 19:26.

  • Mulungu amafunitsitsa kukwanilitsa lonjezo limeneli. Mwacitsanzo, Yehova ‘amalakalaka’ kuukitsa anthu amene anamwalila.—Yobu 14:14, 15.

    Baibo imakambanso kuti Yesu, Mwana wa Mulungu, anacilitsa odwala. N’cifukwa ciani anacita zimenezo? Cifukwa cakuti n’zimene iye anali kufuna. (Maliko 1:40, 41) Monga Atate wake, Yesu anali wofunitsitsa kuthandiza anthu ovutika.—Yohane 14:9.

    Conco, sitikukaika kuti onse aŵili, Yehova ndi Yesu, amafuna kutithandiza kuti tikakhale ndi moyo wabwino mtsogolo.—Salimo 72:12-14; 145:16; 2 Petulo 3:9.

GANIZILANI FUNSO ILI

Munthu aloza pa vesi m’Baibo

Kodi Mulungu adzasintha bwanji dziko lathu kuti likhale labwino?

Baibo imayankha funso limenelo pa MATEYU 6:9, 10 ndi pa DANIELI 2:44.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani