LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • T-33 masa. 1-4
  • Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli?
  • Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Zinthu Zidzakhala Bwanji Mtsogolo?
    Kodi Zinthu Zidzakhala Bwanji Mtsogolo?
  • Kodi Ufumu wa Mulungu Ndi Ciani?
    Kodi Ufumu wa Mulungu Ndi Ciani?
  • Kodi N’zoona Kuti Akufa Angakhalenso ndi Moyo?
    Kodi N’zoona Kuti Akufa Angakhalenso ndi Moyo?
  • Kodi Mavuto Adzathadi?
    Kodi Mavuto Adzathadi?
Onaninso Zina
Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli
T-33 masa. 1-4

Kodi Ndani Maka-maka Amene Akulamulila Dzikoli?

Kodi muganiza kuti ndi . . .

  • Mulungu?

  • anthu?

  • wina wake?

ZIMENE BAIBO IMANENA

“Dziko lonse lili m’manja mwa woipayo.”—1 Yohane 5:19.

“Mwana wa Mulungu anabwela . . . kuti aononge nchito za Mdyelekezi.”—1 John 3:8, New Century Version.

UBWINO WOKHULUPILILA ZIMENEZI

Mudzamvetsetsa cifukwa cake padziko pali mavuto.—Chivumbulutso 12:12.

Mudzakhala ndi ciyembekezo cakuti zinthu padziko zidzakhala bwino mtsogolo.—1 Yohane 2:17.

Satana akulamulila ndale, asilikali, zipembedzo ndi anthu

KODI TINGAKHULUPILILEDI ZIMENE BAIBO IMANENA?

Inde, pa zifukwa zitatu izi:

  • Ulamulilo wa Satana udzaonongedwa. Yehova ndi wokonzeka kwambili kucotsa ulamulilo wa Satana padziko lapansi. Iye walonjeza kuti ‘adzaononga Mdyelekezi’ ndi kukonzanso zinthu zonse zimene Satana waononga.—Aheberi 2:14, Baibulo la Dziko Latsopano.

  • Mulungu wasankha Yesu Kristu kukhala wolamulila wa dziko. Yesu ndi wosiyana kwambili ndi wolamulila wa dzikoli amene ndi wankhanza ndi wodzikonda. Ponena za ulamulilo wa Yesu, Mulungu walonjeza kuti: “Adzamvela cisoni munthu wonyozeka ndi wosauka . . . Adzaombola miyoyo yao ku cipsinjo ndi ciwawa.”—Salimo 72:13, 14.

  • Mulungu sanama. Baibo imakamba mosapita m’mbali kuti: “N’zosatheka kuti Mulungu aname.” (Aheberi 6:18) Yehova akalonjeza zinthu, zimakhala monga kuti zacitika kale. (Yesaya 55:10, 11) ‘Wolamulila wa dzikoli adzaponyedwa kunja.’—Yohane 12:31.

GANIZILANI FUNSO ILI

Banja lacimwemwe lapita kukasangalala pamodzi

Kodi dzikoli lidzakhala bwanji wolamulila wake akacotsedwapo?

Baibo imayankha funso limeneli pa SALIMO 37:10, 11 ndi pa CHIVUMBULUTSO 21:3, 4.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani