LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lfb phunzilo 31 tsa. 78
  • Yoswa na Agibeoni

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Yoswa na Agibeoni
  • Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Agibeoni Anzelu
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Dzuŵa Liimilila
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
lfb phunzilo 31 tsa. 78
Agibeoni avala vovala vong’ambika-ng’ambika, ndipo akamba na Yoswa na asilikali ake

PHUNZILO 31

Yoswa na Agibeoni

Mbili ya kuwonongedwa kwa Yeriko inamveka ku mitundu ina ya m’dziko la Kanani. Mafumu awo anagwilizana kuti akamenyane na Aisiraeli. Koma Agibeoni anapanga pulani. Atavala vovala vong’ambika-ng’ambika anapita kwa Yoswa. Iwo anati kwa iye: ‘Tacokela kudziko lakutali ngako. Tinamva za Yehova, na zonse zimene anakucitilani ku Iguputo na ku Mowabu. Lonjezani kuti simudzatipha, ndipo ife tidzakhala atumiki anu.’

Yoswa anawakhulupilila na kuwalonjeza kuti sadzawapha. Koma patapita masiku atatu, Yoswa anadziŵa zakuti iwo sanacokele kudziko lakutali. Anali kukhala m’dziko la Kanani mmenemo. Conco, Yoswa anafunsa Agibeoni kuti: ‘N’cifukwa ciani munatinamiza?’ Iwo anayankha kuti: ‘Cifukwa tinacita mantha! Tidziŵa kuti Yehova Mulungu wanu ndiye akukumenyelani nkhondo. Conde musatiphe.’ Yoswa anasunga lonjezo lake, cakuti sanawaphe.

Pasanapite nthawi, mafumu asanu acikanani, na magulu awo a asilikali, anagwilizana zokathila nkhondo Agibeoni. Yoswa atamva zimenezi, anatenga asilikali ake na kuyenda usiku wonse kuti akapulumutse Agibeoni. Nkhondo inayamba m’mawa mwake kuseni-seni. Akanani anayamba kubalalika, aliyense kuloŵela kwake. Koma kulikonse kumene anathaŵila, Yehova anali kuwagwetsela vimiyala va matalala. Kenako Yoswa anapempha Yehova kuti aimitse dzuŵa. N’cifukwa ciani Yoswa anapempha Yehova kuimitsa dzuŵa, zimene sizinacitikepo cikhalile? Cifukwa anali kukhulupilila Yehova. Ndipo dzuŵa silinaloŵedi tsiku lonselo, mpaka Aisiraeli anagonjetsa mafumu acikananiwo, na magulu awo a nkhondo.

Yoswa ayang’ana kumwamba na kupempha Yehova kuti aimitse dzuŵa

“Tangotsimikizani kuti mukati ‘Inde’ akhaledi inde, ndipo mukati ‘Ayi’ akhaledi ayi, pakuti mawu owonjezela pamenepa acokela kwa woipayo.”—Mateyu 5:37

Mafunso: Kodi Agibeoni anacita ciani kuti adziteteze? Nanga Yehova anathandiza bwanji Aisiraeli?

Yoswa 9:1–10:15

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani