Mawu Oyamba a Cigawo 2
N’cifukwa ciani Yehova anabweletsa cigumula cimene cinawononga anthu m’nthawi yakale? Kuciyambi kwa mbili ya anthu, Satana anapandukila Yehova. Anthu ena monga Adamu, Hava, na mwana wawo Kaini, anasankha kukhala ku mbali yoipa ya Satana. Koma anthu ena ocepa, monga Abele na Nowa, anasankha kukhala ku mbali yabwino ya Yehova. Anthu ambili anakhala oipa kwambili, cakuti Yehova anaŵawononga onse. Cigawo cino, cidzatithandiza kudziŵa kuti Yehova amaona mbali imene tasankha. Ndipo sadzalola anthu oipa kugonjetsa anthu abwino.