LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lfb masa. 106-107
  • Mawu Oyamba a Cigawo 8

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mawu Oyamba a Cigawo 8
  • Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Kacisi wa Yehova
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Kodi Nthawi Zina Umaona kuti Uli Wekha Ndipo Ukucita Mantha?
    Phunzitsani Ana Anu
  • Solomo Amanga Kacisi
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
lfb masa. 106-107
Mfumu Solomo apeza mayi weni-weni wa mwanayo

Mawu Oyamba a Cigawo 8

Yehova anadalitsa Solomo mwa kum’patsa nzelu zoculuka, na mwayi womanga kacisi. Koma m’kupita kwa nthawi, iye anasiya Yehova. Ngati ndimwe kholo, m’fotokozeleni mwana wanu zimene zinapangitsa Solomo kuti asiye Mulungu. Ufumu unagaŵika, ndipo mafumu oipa anapangitsa mtundu wa Isiraeli kupanduka na kuyamba kulambila mafano. Pa nthawi imeneyo, aneneli a Yehova ambili okhulupilika anazunzidwa na kuphedwa. Mfumukazi Yezebeli anapangitsa kuti ufumu wa kumpoto uloŵelele m’kulambila mafano. Imeneyi inali nthawi yovuta kwambili kwa Aisiraeli. Koma pakati pa Aisiraeli, panali atumiki a Yehova ambili okhulupilika. Ena a iwo anali Mfumu Yehosafati na mneneli Eliya.

MAPHUNZILO AKULU-AKULU M’CIGAWOCI

  • Tumikilani Yehova mokhulupilika, olo ngati a m’banja lanu na anzanu samutumikila

  • Mukam’siya Yehova, palibe cidzakuyendelani bwino. Koma ngati m’mamatila kwa iye, adzakudalitsani

  • Pamene zinthu zakuvutani kwambili, dalilani Yehova. Mwa mphamvu zake, adzakuthandizani m’njila imene simunali kuganizila

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani