LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • th phunzilo 11 tsa. 14
  • Kukamba Mwaumoyo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kukamba Mwaumoyo
  • Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Nkhani Zofanana
  • Yesetsani Kuwafika pa Mtima Omvela
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Kambani Mwaumoyo Pophunzitsa
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Mzimu Waubwenzi na Cifundo
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Nkhani Yophunzitsadi Kanthu Omvela
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
Onaninso Zina
Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
th phunzilo 11 tsa. 14

PHUNZILO 11

Kukamba Mwaumoyo

Lemba losagwila mawu

Aroma 12:11

ZOFUNIKILA: Muzikamba mwaumoyo kuti omvela anu akhale ogalamuka komanso olimbikitsidwa.

MOCITILA:

  • Kambani mocokela pa mtima. Pokonzekela nkhani kapena ulaliki wanu, ganizilani za kufunika kwa uthenga wanu. Idziŵeni bwino nkhani yanu cakuti mukaikambe mocokela pa mtima.

  • Ganizilani omvela anu. Ganizilani za mmene mfundo zimene mudzaŵelenga kapena kuphunzitsa zingapindulitsile ena. Onani njila imene mungazifotokozele mowafika pa mtima omvela anu.

  • Ikani umoyo m’nkhani yanu. Kambani mwaumoyo, osati mopola. Pangani magesca acibadwa, komanso nkhope izionetsa mmene mukumvelela.

    Tumalangizo tothandizila

    Osadabwitsa omvela anu mwa kulankhula na gesica imodzi-modzi osasinthako. Pangani magesca atanthauzo. Kambani mwaumoyo maka-maka pamene mwafika pa mfundo yaikulu, komanso pofuna kulimbikitsa omvela anu kucitapo kanthu. Komabe, musawalemetse omvela anu mwa kulankhula motentha kwambili m’nkhani yanu yonse.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani