LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • th phunzilo 18 tsa. 21
  • Nkhani Yophunzitsadi Kanthu Omvela

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Nkhani Yophunzitsadi Kanthu Omvela
  • Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Nkhani Zofanana
  • Kukamba Mwaumoyo
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Yesetsani Kuwafika pa Mtima Omvela
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Kumveketsa Phindu ya Nkhani
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Kumveketsa Bwino Cifukwa Coŵelengela Lemba
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
Onaninso Zina
Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
th phunzilo 18 tsa. 21

PHUNZILO 18

Nkhani Yophunzitsadi Kanthu Omvela

Lemba losagwila mawu

1 Akorinto 9:19-23

ZOFUNIKILA: Kambani mwa njila yopangitsa omvela anu kuganizilapo pa nkhaniyo, na kuona kuti aphunzilapodi kanthu.

MOCITILA:

  • Ganizilani zimene omvela anu amazidziŵa kale. M’malo mongobweleza zimene iwo anamvelapo kale, athandizeni kuona nkhaniyo mwatsopano.

    Tumalangizo tothandizila

    Musacedwepo kwambili pa mfundo zodziŵika kale, koma dekhani pofotokoza mfundo zatsopano.

  • Fufuzani na kusinkha-sinkha. Ngati n’kotheka, phatikizanipo mfundo zomvekako zacilendo, kapena zocitika za pa nyuzi monga zitsanzo pofuna kumveketsa mfundo zazikulu. Ganizilani mozama mmene zitsanzo zimenezo zikugwilizanila na nkhani yanu.

    Practical tip

    Pokonzekela nkhaniyo, tsitsimulani kaganizidwe kanu mwa kudzifunsa mafunso monga akuti ‘cifukwa ciani, liti, kuti, ndani, komanso motani.’ Kometselani kaphunzitsidwe kanu mwa kuyankha ena mwa mafunso amenewo pokamba nkhani yanu.

  • Onetsani phindu ya nkhani yanu. Unikani mmene mfundo za m’Malemba zingathandizile omvela anu mu umoyo wawo wa tsiku na tsiku. Fotokozani mikhalidwe yakuti-yakuti, kapena maganizo, kapenanso zocitika zoyenelela kwa omvela anu.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani