LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w13 10/1 tsa. 3
  • N’cifukwa Ciani Mufunikila Kucita Cidwi ndi Baibo?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • N’cifukwa Ciani Mufunikila Kucita Cidwi ndi Baibo?
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Nkhani Zofanana
  • N’cifukwa Ciani Muyenela Kuphunzila Baibulo?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Buku Losavuta Kumvetsetsa
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
  • Yehova Mulungu Amakonda Kukamba ndi Anthu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Baibo ni Uthenga wa Mulungu kwa Ife
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
w13 10/1 tsa. 3

NKHANI YA PACIKUTO: KODI BAIBO IMAKAMBA—ZA CIANI?

N’cifukwa Ciani Mufunikila Kucita Cidwi ndi Baibo?

Baibo ndi buku lofala kwambili kuposa buku lililonse padziko lapansi. N’cifukwa ciani zili conco? Cifukwa cimodzi n’cakuti ndi yosavuta kuimvetsetsa. Imafotokoza nkhani zokhudza anthu eni-eni, mmene io anali kukhalila ndi anzao ndiponso ubwenzi wao ndi Mulungu. Nkhani zimenezi zimatiphunzitsa mfundo zothandiza mwa kugwilitsila nchito mau osavuta kumva ndi olunjika. Ndiponso zingatembenuzidwe m’zinenelo zambili cakuti anthu padziko lonse angazimvetsetse mosavuta. Ndipo mfundo za m’Baibo n’zothandiza nthawi zonse.

Koposa zonse, Baibo ndi buku limene limafotokoza za Mulungu, ndipo linacokela kwa Mulungu. Imatiuza dzina la Mulungu, makhalidwe ake ndi colinga cimene analengela dziko lapansi ndi anthu. Baibo imafotokoza mmene Satana anatsutsila ulamulilo wabwino wa Yehova, mmene Yehova adzaonetsela kuti Satana ndi wabodza ndiponso mmene Iye adzathetsela kuipa konse. Kuŵelenga Baibo ndi mtima wofuna kudziŵa zambili kungatithandize kukhala ndi cikhulupililo ndi ciyembekezo.

Baibo imafotokoza zinthu zimene sitingaphunzile kwina kulikonse. Mwacitsanzo, Baibo imatiuza coonadi pankhani monga izi:

▪ Kumene tinacokela ndiponso cifukwa cake timavutika

▪ Zimene Mulungu wakonza kuti apulumutse anthu

▪ Zimene Yesu anaticitila

▪ Zimene zidzacitikila dziko ndi anthu mtsogolo

Bwanji osapatula nthawi kuti muŵelenga masamba otsatila kuti muidziŵe bwino Baibo?

[Bokosi papeji 3]

DZIŴANI IZI PONENA ZA BAIBO

Nkhani yake yaikulu: Mmene Ufumu wakumwamba wa Mulungu udzabweletsela cilungamo ndi mtendele padziko lapansi

Za mkati: Ili ndi mabuku 39 olembedwa m’Ciheberi (mbali zina zocepa zinalembedwa m’Ciaramu) ndipo ena 27 analembedwa m’Cigiriki

Kulembedwa kwake: Inalembedwa ndi amuna 40 kwa zaka zoposa 1,600, kucokela mu 1513 B.C.E. mpaka ca ku ma 98 C.E.

Zinenelo: Baibo yonse kapena mbali yake, yatembenuzidwa m’zinenelo zoposa 2,500

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani