Zamkati
October 1, 2013
Kodi Baibo Imakamba—Za Ciani?
© 2013 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania. All rights reserved.
NKHANI ZOPHUNZILA
DECEMBER 2-8, 2013 | TSAMBA 9 • NYIMBO: 110, 15
Cilengedwe Cimadziŵikitsa Mulungu Wamoyo
Mulungu amene saoneka analenga cilengedwe conse cimene timaona. Kodi inu mumakhulupilila zimenezi ndi mtima wonse? Koma si anthu onse amene amakhulupilila zimenezi. Kodi tingathandize bwanji anthu ena kumvetsa coonadi ponena za Mlengi ndiponso kulimbitsa cikhulupililo cathu mwa iye? Nkhani iyi idzafotokoza mmene tingacitile zimenezi.
DECEMBER 9-15, 2013 | TSAMBA 14 • NYIMBO: 62, 84
“Tumikilani Yehova Monga Akapolo”
Akristu amalangizidwa kutumikila Yehova monga akapolo. M’nkhani ino tidzaphunzila zokhudza ufulu umene akapolo anali nao malinga ndi Cilamulo ca Mose. Tidzaphunzilanso mmene ife tingapewele kukhala akapolo a Satana ndi zinthu zokopa za m’dziko lake, ndiponso mapindu oculuka amene timapeza ngati titumikila Mulungu monga akapolo.
DECEMBER 16-22, 2013 | TSAMBA 19 • NYIMBO: 68, 6
Zimene Tingaphunzilepo pa Pemphelo Lokonzedwa Bwino
DECEMBER 23-29, 2013 | TSAMBA 24 • NYIMBO: 57, 56
Citani Zinthu Mogwilizana ndi Pemphelo la Yesu
Ngati nthawi zonse tisinkha-sinkha Mau a Mulungu, mapemphelo athu adzakhala atanthauzo. Nkhani yoyamba ifotokoza mmene kucita zimenezi kunathandizila Alevi kupeleka pemphelo latanthauzo m’malo mwa anthu a Mulungu. Yaciŵili idzafotokoza mmene tingacitile zinthu mogwilizana ndi limodzi mwa mapemphelo a Yesu ocokela pansi pa mtima. Mapemphelo onse amenewa amatiphunzitsa kuika cifunilo ca Yehova patsogolo pa zofuna zathu.
NKHANI ZINA M’MAGAZINI INO
N’cifukwa Ciani Mufunikila Kucita Cidwi ndi Baibo? 3
Mulungu Anakonza Njila Yopulumutsila Anthu 5
Uthenga Wabwino wa Anthu Onse 7