LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w13 10/1 tsa. 4
  • Kodi Tinacokela Kuti?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Tinacokela Kuti?
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Cifunilo ca Mulungu Kwa Anthu N’ciani?
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • Kodi Zoipa Komanso Mavuto Zinakhalako Bwanji?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Kodi Mulungu Ali Nalo Colinga Canji Dziko Lapansi?
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Kodi Umoyo Unali Bwanji m’Paladaiso?
    Mvetselani kwa Mulungu Kuti Mukhale ndi Moyo Wamuyaya
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
w13 10/1 tsa. 4

Kodi Tinacokela Kuti?

Buku loyamba m’Baibo limene ndi Genesis, limafotokoza mwacidule ciyambi ca cilengedwe conse kuti: “Paciyambi Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.” (Genesis 1:1) Pambuyo polenga zomela ndi nyama, Mulungu analenga anthu oyambilila, Adamu ndi Hava. Iwo anali osiyana ndi nyama cifukwa cakuti anali ndi makhalidwe ofanana ndi a Mulungu, kuphatikizapo ufulu wodzisankhila zocita. Conco, zosankha zao zikanapangitsa kuti aimbidwe mlandu kapena kudalitsidwa. Iwo akanamvela malangizo a Mulungu, akanakhala makolo a anthu onse amene anayenela kusangalala ndi mtendele ndiponso moyo wangwilo padziko lapansi kwamuyaya mogwilizana ndi cifunilo ca Mulungu.

Komabe, mngelo wina kapena kuti colengedwa cauzimu, anagwilitsila nchito anthu kuti akwanilitse zofuna zake zadyela. Conco, iye anakhala Satana kutanthauza “Wotsutsa.” Mwa kugwilitsila nchito njoka, Satana ananamiza Hava kuti angakhale ndi moyo wabwino popanda kudalila Mulungu. Adamu ndi Hava anamvela Satana, ndipo anaononga ubwenzi wao ndi Mlengi wao. Cifukwa cosankha molakwika, makolo athu oyambilila anataya mwai wokhala ndi moyo wamuyaya, ndipo anapatsila ife tonse ucimo, kupanda ungwilo ndi imfa.

Mwamsanga, Mulungu analengeza cifunilo cake cothetsa mavuto amenewa kuti apeleke kwa mbadwa za Adamu mwai wokhala ndi moyo wamuyaya. Mulungu ananenelatu kuti “mbeu,” kutanthauza munthu wina wapadela, adzaononga Satana ndi kucotsapo mavuto onse amene Satana, Adamu ndi Hava anabweletsa. (Genesis 3:15) Kodi ndani amene anali kudzakhala “mbeu” imeneyo? Zimenezi zinadziŵika patapita nthawi.

Komabe, Satana nthawi zonse anali kuyesa-yesa kulepheletsa cifunilo cabwino ca Mulungu. Ucimo ndi kuipa zinafalikila kwambili. Mulungu anaganiza zoononga anthu oipa ndi cigumula. Iye analamula Nowa munthu wolungama kumanga cingalawa cacikulu, kuti iye ndi banja lake akapulumuke pamodzi ndi nyama zimene anauzidwa kuloŵetsa m’cingalawa.

Pambuyo pa caka cimodzi Cigumula citayamba, Nowa ndi banja lake anatuluka m’cingalawa ndi kukhala pa dziko loyeletsedwa. Koma “mbeu” imeneyo inali isanadziŵike.

—Yazikidwa pa Genesis caputala 1 mpaka 11; Yuda 6, 14, 15; Chivumbulutso 12:9.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani