LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w15 1/1 tsa. 16
  • Kuyankha Mafunso A m’Baibulo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuyankha Mafunso A m’Baibulo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Zofanana
  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Kuyankha Mafunso A M’baibulo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
  • Kodi Moyo Unayamba Bwanji?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Mulungu Anapanga Kumwamba na Dziko Lapansi
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 1/1 tsa. 16

Kuyankha Mafunso A m’Baibulo

N’ciani cimacititsa anthu ambili kuganizila zakuti kuli Mlengi?

Amai akunyadila mwana wao

Kodi zamoyo si zodabwitsa?

Zaka 3,000 zapitazo, wolemba ndakatulo wina anati: “Munandipanga modabwitsa ndipo zimenezi zimandicititsa mantha.” (Salimo 139:14) Kodi sizimakucititsani mantha mukaganizila mmene mwana wakhanda amakulila kucokela ku selo limodzi? Anthu ambili amakamba kuti pali Mlengi amene anapanga zamoyo.—Ŵelengani Salimo 139:13-17; Aheberi 3:4.

Amene analenga cilengedwe conse ndi kupanga dziko lapansi ndi amene analenganso zamoyo zonse. (Salimo 36:9) Iye analankhula ndi anthu ndipo anatiuza zinthu zokhudza iye.—Ŵelengani Yesaya 45:18.

Kodi tinacokela ku nyama?

Matupi athu ndi ofanana ndi a nyama m’mbali zambili. Izi zili conco, cifukwa cakuti anthu ndi nyama anapangidwa ndi Mlengi kuti azikhala padziko lapansi. Mulungu sanapange munthu woyamba kucokela ku nyama koma ku fumbi lapansi.—Ŵelengani Genesis 1:24; 2:7.

Anthu amasiyana ndi nyama m’njila ziŵili zazikulu. Yoyamba, anthu amatha kudziŵa zinthu, kuonetsa cikondi ndi kulemekeza Mlengi. Yaciŵili, nyama sizinalengedwe kuti zizikhala kosatha, koma anthu analengedwa kuti azitelo. Anthu onse amafa cifukwa cakuti munthu woyamba anakana kutsogoleledwa ndi Mlengi.—Ŵelengani Genesis 1:27; 2:15-17.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 1 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Buku limeneli lipezekanso pa Webusaiti ya www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani