LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w15 11/1 tsa. 16
  • Kuyankha Mafunso a M’baibulo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuyankha Mafunso a M’baibulo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Yesu Adzacita Ciani Mtsogolo?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Yesu Adzathetsa Umphawi
    Nkhani Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 11/1 tsa. 16

Kuyankha Mafunso a M’baibulo

Kodi n’zotheka kukhala m’dziko lopanda umphawi?

Mkazi wanyamula mbale yopanda kanthu, ndipo wakumbatila kamtsikana

Kodi Mulungu adzathetsa bwanji umphawi padzikoli?—Mateyu 6:9, 10.

Anthu mamiliyoni amafa caka ciliconse cifukwa ca matenda obwela kaamba ka kucepelekela kwa cakudya. Ngakhale kuti maiko ambili ndi olemela, anthu oculuka ali mu umphawi wadzaoneni. Baibulo limatiuza kuti umphawi wavutitsa anthu kwa nthawi yaitali.—Ŵelengani Yohane 12:8.

Kuti umphawi uthe, pafunika boma lamphamvu la padziko lonse limene lingagaŵe cuma ca dziko mosakondela. Boma limenelo lidzafunika kuthetsa nkhondo cifukwa ndilo vuto lalikulu limene limacititsa umphawi. Mulungu walonjeza boma la padziko lonse limene lidzathetsa mavuto onse.—Ŵelengani Daniel 2:44.

Ndani angathetse umphawi?

Mulungu wasankha Mwana wake, Yesu, kuti adzalamulile anthu onse. (Salimo 2:4-8) Yesu adzapulumutsa anthu osauka ndipo adzathetsa kupondelezana komanso ciwawa.—Ŵelengani Salimo 72:8, 12-14.

Yesu, monga “Kalonga Wamtendele,” adzakhazikitsa mtendele ndi citetezo padziko lonse lapansi. Anthu onse padziko lapansi adzakhala ndi nyumba zaozao, adzasangalala kugwila nchito yokhutilitsa, ndipo adzakhala ndi cakudya coculuka.—Ŵelengani Yesaya 9:6, 7; 65:21-23.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 8 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mungatengenso buku limeneli pa www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani