LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 11/13 tsa. 2
  • Bokosi La Mafunso

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Bokosi La Mafunso
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Nkhani Zofanana
  • Ndi pa Zocitika Ziti Pamene Mlongo Ayenela Kuvala Cophimba Kumutu, Ndipo N’cifukwa Ciani?
    “Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
  • Mafunso Ocokela Kwa Aŵelengi
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Tizionetsa Ulemu Tikafika pa Khomo la Munthu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Kuyambitsa Phunzilo la Baibulo Pogwilitsila Nchito Kabuku ka Uthenga Wabwino Wocokela Kwa Mulungu
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
km 11/13 tsa. 2

Bokosi La Mafunso

◼ Kodi mlongo ayenela kuvala cakumutu pamene apita ndi m’bale kuphunzilo la Baibo locititsa coimilila pakhomo?

Ngati mlongo acititsa phunzilo la Baibo lokhazikika ndipo m’bale wobatizika alipo, mlongo ayenela kuvala cakumutu. (1 Akor. 11:3-10) Nsanja ya Olonda ya July 15, 2002, tsamba 27 inafotokoza kuti: ‘Kumeneku n’kuphunzitsa kumene amakhala atakonzelatu ndipo wocititsa phunziloyo amatsogolela ndithu. Pa zocitika ngati zimenezi, phunzilo limenelo limakhala mbali yoonjezela ya maphunzilo a mpingo. Ngati mlongo acititsa phunzilo lotelo ndipo m’bale alipo, mlongo ayenela kuvala cakumutu.’ Mlongo adzafunikanso kuvala cakumutu ngati atsogoza phunzilo pamodzi ndi mwamuna amene ndi wofalitsa wosabatizika. Iye afunika kucita zimenezi kaya atsogozela phunzilo m’nyumba, coimilila pakhomo kapena kwina kulikonse.

Ndipo ngati phunzilo la Baibo locititsa coimilila pakhomo silinakhazikitsidwe, mlongo sangavale cakumutu ngakhale pamene m’bale alipo. Iye sangavale cakumutu ngakhale kuti colinga ca ulendo wobwelelako ndi kusonyeza mocitila phunzilo la Baibo kapena kukambilana nkhani yocokela m’zofalitsa zogwilitsila nchito pophunzitsa. Popeza pamafunika kupanga maulendo obwelelako angapo tisanakhazikitse phunzilo la Baibo locititsa coimilila pakhomo, ofalitsa adzafunika kuona pamene kungakhale koyenela kuvala cakumutu.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani