LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 July tsa. 8
  • Tizionetsa Ulemu Tikafika pa Khomo la Munthu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Tizionetsa Ulemu Tikafika pa Khomo la Munthu
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Kuyambitsa Phunzilo la Baibulo Pogwilitsila Nchito Kabuku ka Uthenga Wabwino Wocokela Kwa Mulungu
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Bokosi La Mafunso
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Muzionetsa Khalidwe Lopambana mu Ulaliki
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 July tsa. 8

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Tizionetsa Ulemu Tikafika pa Khomo la Munthu

M’bale waimilila pa khomo la munthu, m’bale asonjola pa windo, m’bale akudya, m’bale alemba meseji

Akhristu ali monga “coonetsedwa m’bwalo la maseŵela kudziko.” (1 Akor. 4:9) Conco, sitiyenela kudabwa kuti anthu ena amationela pa windo kapena kumvetsela ali kumbuyo kwa citseko. Pa nyumba zina pangakhale makamela acitetezo kapena maikilofoni yothandiza mwini nyumba kutiona, kutimvetsela, kapena kutijambula mau. Nazi njila zina zotithandiza kuonetsa ulemu tikafika pakhomo la munthu.—2 Akor. 6:3.

ZOCITA ZANU (Afil. 1:27):

  • Muzilemekeza mwini nyumba mwa kusasuzila kapena kusonjola m’nyumba mwake. Muzipewa kudya, kumwa, kapena kutuma foni na kulemba meseji muli imilile pakhomo la munthu

MAU ANU (Aef. 4:29):

  • Pamene muli pakhomo la munthu, samalani kuti musakambe zinthu zimene simufuna kuti mwini nyumba amveleko. Pofuna kuika maganizo pa zimene adzakamba, ofalitsa ena amalekeza kukambilana nkhani zawo

Abale aŵili aimilila mwaulemu pa nyumba ya munthu ndipo mwininyumba awasonjolela

Ni njila zina ziti zimene mungaonetsele makhalidwe abwino ngati mwafika pakhomo la munthu?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani