LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb16 March tsa. 2
  • Landilani Alendo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Landilani Alendo
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
  • Nkhani Zofanana
  • Alandileni!
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Alandileni Bwino
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Kucelezana ni Khalidwe Lofunika Kwambili
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • Ciitano Capadela ca Yehova Cokhala Alendo Ake
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
mwb16 March tsa. 2

UMOYO WATHU WACIKRISTU

Landilani Alendo

Pa March 23, anthu oposa 12 miliyoni adzabwela ku Cikumbutso monga alendo athu. Iwo adzamvetsela kwa mkambi amene adzafotokoza mphatso ya dipo imene Yehova watipatsa, ndi madalitso ena a mtsogolo amene anthu adzalandila. (Yes. 11:6-9; 35:5, 6; 65:21-23; Yoh. 3:16) Komabe, si mkambi cabe amene adzacitila umboni pa cocitika capadela cimeneci. Tonsefe tidzakhala ndi mwai wolandila alendo. (Aroma 15:7) Onani zimene tifunika kucita.

Wa Mboni za Yehova akulandila mlendo pa Cikumbutso; wa Mboni za Yehova akuŵelengela pamodzi Baibulo ndi alendo pa Cikumbutso
  • M’malo mongokhala pampando ndi kuyembekezela pulogalamu kuti iyambe, landilani alendo ndiponso anthu ofooka mwa kumwetulila ndi kuwapatsa moni mwaubwenzi

  • Mukamalandila mabwenzi amene munaitanila, mulandilenso ena amene abwela cifukwa cakuti analandila kapepala ka ciitano. Pemphani atsopano kuti mukhale nao pamodzi, ndipo ŵelengani nao pamodzi Baibulo ndi kuona nao m’buku lanu nyimbo

  • Nkhani ikatha, khalani wofunitsitsa kuyankha mafunso amene angakhale nao. Ngati mpingo wanu uyenela kucoka pa Nyumba ya Ufumu mwamsanga kuti ena asonkhanilanepo, pangani makonzedwe akuti mukaonane ndi munthuyo mwamsanga. Ngati simudziŵa kumene akhala, mungamuuze kuti: “Ndingakonde kumva mmene mwaonela msonkhanowu. Kodi ndingakupezeni bwanji?”

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani