LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 June tsa. 3
  • Mau Onse a Yehova Amakwanilitsika

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mau Onse a Yehova Amakwanilitsika
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 June tsa. 3

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU | YEREMIYA 51-52

Mau Onse a Yehova Amakwanilitsika

Yehova ananenelatu mwatsatane-tsatane zinthu zimene zidzacitika mtsogolo

Msilikali woponya mivi wolondela nyumba ya Mfumu yaciperesiya

Msilikali woponya mivi wolondela nyumba ya Mfumu yaciperesiya

“Nolani mivi yanu”

51:11, 28

  • Amedi ndi Aperisi anali akatswili oponya mivi, ndipo uta ndiwo unali cida cawo codalilika. Anali kunola kwambili mivi yawo kuti akalasa, iziloŵa mozama m’thupi

“Amuna amphamvu a ku Babulo asiya kumenya nkhondo”

51:30

  • Zolemba za Nabonidus Chronicle zimati: “Asilikali a Koresi analoŵa mu Babulo popanda kucita nkhondo.” Izi zigwilizana na ulosi wa Yeremiya

Nabonidus Chronicle

Nabonidus Chronicle

“Babulo adzakhala milu yamiyala [ndiponso] bwinja mpaka kalekale”

51:37, 62

  • Kuyambila mu 539 B.C.E., ulemelelo wa Babulo unayamba kutha. Alexander Wamkulu anafuna kupanga Babulo kukhala likulu lake, koma anafa mwadzidzidzi. Pamene Cikhristu cinali kuyamba, Ayuda ena anali akali ku Babulo. Ndiye cifukwa cake nthawi zina Petulo anali kupitako. Koma zaka za m’ma 300 C.E., mzindawo unakhala matongwe, ndipo m’kupita kwa nthawi unathelatu

    Chati coonetsa nthawi imene Babulo anagonjetsedwa, imfa ya Alexander wam’kulu, Petulo mu Babulo, matongwe a Babulo

Kodi kukwanilitsika kwa ulosi wa m’Baibo kuyenela kunikhudza bwanji?

Kodi anthu ena ningawaphunzitseko ciani cokhudza ulosiwu?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani