CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | 2 AKORINTO 7-10
Utumiki Wathu Wothandiza Pakacitika Tsoka
8:1-4; 9:7
Akhristufe timacita utumiki wa mbali ziŵili. Mbali yoyamba ni “utumiki wokhazikitsanso mtendele,” kapena kuti nchito yathu yolalikila na kuphunzitsa. Mbali yaciŵili ni “utumiki wothandiza” okhulupilila anzathu. (2 Akor. 5:18-20; 8:4) Conco kuthandiza Akhristu ovutika ni mbali ya utumiki wathu wopatulika. Tikamatengako mbali,
timasamalila bwino zofunika za abale na alongo athu. —2 Akor. 9:12a
timathandiza Akhristu ovutika kuyambanso kucita zinthu zauzimu, zimene ziphatikizapo kugwila nchito yolalikila modzipeleka monga njila yoonetsela ciyamikilo cawo kwa Yehova.—2 Akor. 9:12b
timalemekeza Yehova. (2 Akor. 9:13) Utumiki wathu wothandiza pakacitika tsoka umacitila umboni kwa aliyense, kuphatikizapo anthu amene amaona Mboni za Yehova m’njila yolakwika