LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb19 August tsa. 8
  • Nchito Zabwino Zimene Sizidzaiŵalidwa

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Nchito Zabwino Zimene Sizidzaiŵalidwa
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Beteli n’Ciani?
    Ndani Amene Akucita Cifunilo Ca Yehova Masiku Ano?
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
mwb19 August tsa. 8
Mlongo akuseŵenzela m’khichini pa Beteli

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nchito Zabwino Zimene Sizidzaiŵalidwa

Atumiki onse a Yehova angathe kugwila nchito yopatulika imene iye adzawakumbukila nayo mpaka kale-kale. Monga kholo lacikondi limene limanyadila zimene mwana wake wakwanitsa kucita, Yehova saiŵala nchito yathu na cikondi cimene timaonetsa pa dzina lake. (Mat. 6:20; Aheb. 6:10) N’zoona kuti maluso na zocitika mu umoyo zimasiyana-siyana. Koma ngati ticita zonse zimene tingathe potumikila Yehova, tidzakhala acimwemwe. (Agal. 6:4; Akol. 3:23) Kwa zaka zambili, abale na alongo masauzande akhala akutumikila pa Beteli. Kodi mungadzipeleke kuti mukatumikileko pa Beteli? Ngati simungatelo, bwanji osalimbikitsako wina wake kuti akaciteko utumikiwu, kapena kuthandiza wa m’Banja la Beteli kuti apitilize kutumikila m’njila yapadela imeneyi?

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI DZIPELEKENI KUKACITA UTUMIKI WA PA BETELI, PAMBUYO PAKE YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • N’ciani ciyenela kulimbikitsa munthu kucita utumiki wa pa Beteli?

  • Kodi abale na alongo ena akamba zotani zokhudza madalitso amene apeza cifukwa cotumikila pa Beteli?

  • Kodi pali ziyenelezo zotani za utumiki wa pa Beteli?

  • Mungafunsile motani utumiki wa pa Beteli?

Atumiki a pa Beteli atatu akugwilila nchito pamodzi pa kompyuta; m’bale akulonga mabuku m’mabokosi; m’bale akugwila nchito ya ukalipentala pa Beteli

Ziyenelezo za Utumiki wa pa Beteli

  • Kukonda kwambili Yehova na gulu lake

  • Makhalidwe abwino komanso cikumbumtima coyela pamaso pa Yehova

  • Kuvala na kudzikonza koyenelela Mkhristu

  • Wosankha zosangalatsa zoyenela Mkhristu

  • Nthawi zambili, wa zaka za pakati pa 19 na 35

  • Woganiza bwino ndiponso wa thanzi labwino

  • Wokwanitsa kuŵelenga, kulemba, na kukamba bwino citundu cimene ofesi ya nthambi ya kumaloko imaseŵenzetsa

  • Wokonzeka kutumikila kwa caka cimodzi kapena kuposelapo

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani