LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb19 September tsa. 7
  • “Pitilizani Kuganizila Zimenezi”

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • “Pitilizani Kuganizila Zimenezi”
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • Nkhani Zofanana
  • Kugwilizana Pakati pa Kusunga Umphumphu na Maganizo Athu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Kusinkha-sinkha kwa Mtima Wanga
    ‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
  • Mmene Tingasankhile Zosangalatsa
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
  • Mmene Mungasankhile Zosangulutsa Zabwino
    “Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
mwb19 September tsa. 7
M’bale ali pa kompyuta yake usiku, ndipo mkango wobangula umene ukuimila Satana, uli pa mbali pake

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

“Pitilizani Kuganizila Zimenezi”

Zotani? Afilipi 4:8 ikamba kuti tifunika kuganizila zinthu zilizonse zoona, zilizonse zofunika kwambili, zilizonse zolungama, zilizonse zoyela, zilizonse zacikondi, zilizonse zoyamikilika, khalidwe labwino lililonse, ndi ciliconse cotamandika. Koma izi sizitanthauza kuti Akhristu afunika kumangoganizila za Baibo nthawi zonse. Ngakhale n’conco, zimene timasinkha-sinkha ziyenela kukhala zokondweletsa Yehova. Siziyenela kukhala zimene zingatilepheletse kukhala wokhulupilika kwa iye.—Sal. 19:14.

Kupewa maganizo oipa kumakhala kovuta. Timafunika kulimbana na matupi athu opanda ungwilo komanso Satana, “mulungu wa nthawi ino.” (2 Akor. 4:4) Popeza kuti mphamvu yake imagwila nchito pa zocitika za pa TV, mawailesi, intaneti, ndiponso m’mabuku, zinthu zikuipila-ipila. Ngati sitisankha bwino zinthu zimene tiloŵetsa m’maganizo mwathu, maganizo athu angaipitsidwe, ndipo m’kupita kwa nthawi khalidwe lathu lingasinthe.—Yak. 1:14, 15.

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI MUZIPEWA ZINTHU ZIMENE ZINGAKULEPHELETSENI KUKHALA WOKHULUPILIKA—ZOSANGULUTSA ZOIPA, PAMBUYO PAKE KAMBILANANI MAFUNSO AYA:

  • M’bale akutamba zinthu zoipa pa foni yake pa usiku

    Kodi m’bale anali kutamba ciani pa foni yake? Nanga zinam’khudza bwanji?

  • M’bale akucoka pa malo ocezela apaintaneti

    Kodi malemba aya, Agalatiya 6:7, 8, ndiponso Salimo 119:37 anamuthandiza bwanji?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani