LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb19 October tsa. 8
  • Yehova Amakonda Anthu Aukhondo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Yehova Amakonda Anthu Aukhondo
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • Nkhani Zofanana
  • Mulungu Amakonda Anthu Oyela
    “Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
  • Yehova Amafuna Anthu Ake Kukhala Oyela
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
  • Tiyenela Kucita Ciyani Kuti Tikhale Oyela Pamaso pa Mulungu?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • “Citani Zonse ku Ulemelelo wa Mulungu”
    Gulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
mwb19 October tsa. 8
M’bale akuyeletsa m’toileti pa Nyumba ya Ufumu

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Yehova Amakonda Anthu Aukhondo

“Uzisamba m’manja. Uziyeletsa cipinda cako. Uzipyanga m’mnyumba. Uzitaya vinyalala.” Mwa kukamba mawu amenewa, makolo ambili amaphunzitsa ana awo mmene angakhalile aukhondo. Koma mfundo za kukhala aukhondo zimacokela kwa Mulungu wathu woyela. (Eks. 30:18-20; Deut. 23:14; 2 Akor. 7:1) Ngati timasunga thupi lathu na zinthu zathu mwaukhondo, timalemekeza Yehova. (1 Pet. 1:14-16) Nanga bwanji ponena za nyumba zathu na malo okhala? Mosiyana na anthu amene amataya vinyalala citaye-taye m’njila na m’mapaki, Akhristu amayesetsa kusunga dziko lapansi mwaukhondo. (Sal. 115:16; Chiv. 11:18) Ngakhale kutaya tunthu tung’ono-tung’ono monga tumapepa twa maswiti, mabotolo ya dilinki, kapena mababugamu, kungaonetse mmene timaonela nkhani ya ukhondo. M’mbali zonse za umoyo wathu, tifunika kuonetsa kuti “ndife atumiki a Mulungu.”​—2 Akor. 6:3, 4.

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI, MULUNGU AMAKONDA ANTHU OYELA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • Kodi anthu ena amakamba kuti n’ciani cimawalepheletsa kusunga zinthu zawo mwaukhondo?

  • Kodi Cilamulo ca Mose cinaonetsa bwanji maganizo a Yehova pa nkhani ya ukhondo?

  • Kodi tingacitile bwanji umboni za Yehova popanda kukamba ciliconse?

Tate wakwela m’moto yauve ya mwana wake; tate na mwana akambilana za miyezo ya Yehova pa nkhani ya ukhondo; ansembe aŵili a m’nthawi ya Aisiraeli ali pafupi na beseni ya mkuwa yosambilamo; kagulu ka ulaliki kakutuluka m’motoka yaukhondo ya mwanayo

Kodi ningaonetse bwanji kuti nimatengela maganizo a Yehova pa nkhani ya ukhondo mu umoyo wanga?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani