CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | GENESIS 44-45
Yosefe Anakhululukila Abale Ake
44:1, 2, 33, 34; 45:4, 5
Zingakhale zovuta kukhululuka, maka-maka ngati wina anaticitila zinthu zoipa mwadala. Kodi n’ciani cinathandiza Yosefe kukhululukila abale ake pamene anamucitila zinthu zoipa?
- Yosefe sanafune kuwabwezela, m’malomwake anayetsetsa kuona ngati iwo anasintha popeza anali kufuna kuwakhululukila.—Sal. 86:5; Luka 17:3, 4 
- Yosefe sanapitilize kusunga cakukhosi, m’malomwake anatengela citsanzo ca Yehova amene amakhululukila na mtima wonse. —Mika 7:18, 19 
Kodi ningatengele bwanji citsanzo ca Yehova pankhani yokhululukila ena?