LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 August tsa. 5
  • Tamandani Yehova Monga Mpainiya

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Tamandani Yehova Monga Mpainiya
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Nkhani Zofanana
  • Mipata Yoonjezeka Yotamanda Yehova
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Kodi Mpainiya Ndani?
    Ndani Amene Akucita Cifunilo Ca Yehova Masiku Ano?
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 August tsa. 5
M’bale akuwelengela munthu wina lemba m’mbali mwa nyanja.

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Tamandani Yehova Monga Mpainiya

Aisiraeli anali na zifukwa zabwino zotamandila Yehova. Iye anawatulutsa mu Iguputo na kuwapulumutsa kwa asilikali a Farao. (Eks. 15:1, 2) Yehova wapitiliza kucitila anthu ake zinthu zabwino. Kodi tingaonetse bwanji kuti ndife oyamikila?—Sal. 116:12.

Njila imodzi ni mwa kutumikila monga mpainiya wothandiza kapena wanthawi zonse. Mungapemphele kwa Mulungu kuti akupatseni mtima wofunitsitsa na mphamvu zoti mutumikile monga mpainiya. (Afil. 2:13) Ambili amayamba mwa kucitako upainiya wothandiza. Pocita utumiki waupainiya umenewu, mungasankhe kuthela maola 30 kapena 50 m’mwezi wa March na April, komanso m’mwezi umene woyang’anila dela acezela mpingo. Pambuyo poona cimwemwe cimene mwapeza cifukwa cotumikila monga mpainiya wothandiza, mwina mungafune kulimbikila kuti mutumikile monga mpainiya wanthawi zonse. Ngakhale ena amene agwila nchito yolembedwa kapena amene ali na vuto la thanzi akwanitsa kucita upaniya wanthawi zonse. (mwb16.07 8) Ndithudi timacita zonse zimene tingathe potamanda Yehova. Ndipo ni woyeneladi kutamandidwa.—1 Mbiri 16:25.

TAMBANI VIDIYO YAKUTI ALONGO ATATU A PACIBALE KU MONGOLIA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:

  • Pikica ya m’vidiyo yakuti ‘Alongo Atatu a Pacibale ku Mongolia.’ Undraa, mmodzi wa apainiya amenewa, akufuna kukwela basi.

    Kodi ni zopinga ziti zimene alongo atatu aja anagonjetsa kuti akhale apainiya?

  • Pikica ya m’vidiyo yakuti ‘Alongo Atatu a Pacibale ku Mongolia.’ Oyun, mmodzi wa apainiya amenewa, akusewenzela m’cipinda codyela pa Beteli.

    Nanga ni madalitso otani amene anapeza?

  • Pikica ya m’vidiyo yakuti ‘Alongo Atatu a Pacibale ku Mongolia.’ Dorjkhand, mmodzi wa apainiya amenewa, alalikila kwa mwamuna winawake mu utumiki.

    Ni mwayi wa mautumiki uti umene anapeza pamene anali kutumikila monga apainiya anthawi zonse?

  • Pikica ya m’vidiyo yakuti ‘Alongo Atatu a Pacibale ku Mongolia.’ Apainiya atatu amenewa ali pamodzi na amayi awo.

    Kodi citsanzo cawo cinawakhudza motani ena?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani