LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 September tsa. 3
  • Pewani Kufalitsa Nkhani za Bodza

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Pewani Kufalitsa Nkhani za Bodza
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Nkhani Zofanana
  • “Munthu Amene Sadziŵa Zinthu Amakhulupilila Mau Alionse”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Kodi Mudziŵa Bwino Zoona Zake?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 September tsa. 3

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Pewani Kufalitsa Nkhani Zabodza

Mzimayi wadabwa na zimene waona pa foni yake pamene agula zinthu m’shop.

Masiku ano, nkhani zimafalikila mwamsanga kwa anthu mamiliyoni ambili kupitila m’zopulinta, pa wailesi, pa TV, komanso pa Intaneti. Anthu amene amalambila “Mulungu wacoonadi” amayesetsa kupewa kufalitsa nkhani zabodza, ngakhale mosadziŵa. (Sal. 31:5; Eks. 23:1) Kuuza anthu ena nkhani yabodza kungakhale kovulaza kwambili. Pofuna kutsimikizila ngati nkhani inayake ni yazoona, dzifunseni kuti:

  • ‘Kodi magwelo a nkhaniyi ni odalilika?’ Munthu amene akutiuza nkhani sangadziŵe zeni-zeni zokhudza nkhaniyo. Nkhani zimene zimacoka kwa munthu wina kupita kwa wina nthawi zina zimasintha, conco tifunika kukhala osamala ngati sitidziŵa kumene nkhaniyo inacokela kapena kumene inayambila. Popeza amene ali na maudindo mu mpingo ndiwo gwelo la nkhani zodalilika, iwo afunika kukhala osamala kwambili pankhani youza ena zinthu zopanda umboni.

  • ‘Kodi ni misece?’ Ngati nkhaniyo ni yoipitsa mbili ya munthu wina kapena gulu, n’canzelu kupewa kuuzako ena.—Miy. 18:8; Afil. 4:8.

  • ‘Kodi nkhaniyi ni yazoona?’ Khalani maso pamene mumvela nkhani zokopa.

TAMBANI VIDIYO YAKUTI KODI NINGAKANIZE BWANJI MIJEDO? NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:

  • Mnyamata wamangidwa pa candamale ndipo mipeni ikulasa mbali mwake pa candamaleco.

    Malinga na Miyambo 12:18, kodi mawu athu angavulaze ena motani?

  • Anthu aunjikana pamodzi ndipo akucita mijedo.

    Kodi Afilipi 2:4 ingatithandize bwanji kuti tizikamba zinthu zoyenela zokhudza anthu ena?

  • Munthu wina akukana kumvetsela mijedo imene wina akumuuza.

    Kodi tifunika kucita ciani pamene ena ayamba kukamba nkhani zolakwika zokhudza anthu ena?

  • Munthu wina akukamba mijedo pamene wina monga wocitila lipoti akulemba zimene zikukambidwazo.

    Tisanayambe kukamba zokhudza ena, ni mafunso ati amene tifunika kudzifunsa?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani