LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb22 March tsa. 15
  • Thandizani Maphunzilo a Baibo Kukhala pa Ubale Wolimba na Yehova

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Thandizani Maphunzilo a Baibo Kukhala pa Ubale Wolimba na Yehova
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Nkhani Zofanana
  • Thandizani Maphunzilo a Baibo Kuleka Makhalidwe Odetsa
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Phunzitsani Maphunzilo Anu a Baibo Kudzidyetsa Okha Mwauzimu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Funsani Mafunso
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Afikeni Pamtima Anthu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
mwb22 March tsa. 15

CITANI KHAMA PA ULALIKI | WONJEZELANI CIMWEMWE CANU MU ULALIKI

Thandizani Maphunzilo a Baibo Kukhala pa Ubale Wolimba na Yehova

Yehova amafuna kuti tizim’tumikila cifukwa com’konda. (Mat. 22:37, 38) Kukonda Mulungu n’kumene kudzalimbikitsa ophunzila Baibo kupanga masinthidwe ofunikila, na kukhalabe olimba akakumana na mayeso. (1 Yoh. 5:3) Cikondi cawo pa Mulungu n’cimene cidzawalimbikitsa kuti abatizike.

Thandizani ophunzila anu kuona kuti Mulungu amawakonda. Afunseni mafunso monga awa: “Kodi izi zikuphunzitsani ciani za Yehova?” kapena “Kodi izi zimaonetsa bwanji kuti Mulungu amakukondani?” Athandizeni kuona mmene Yehova akuwathandizila pa umoyo wawo. (2 Mbiri 16:9) Auzeni mmene Yehova wayankhila mapemphelo anu acindunji, ndipo alimbikitseni kuona mmene Yehova amayankhila mapemphelo awo. Timakondwela kuona kuti ophunzila Baibo ayamba kumva kuti Yehova amawakonda, ndipo nawonso akuonetsa cikondi cawo pa iye.

ONELELANI VIDIYO YAKUTI THANDIZANI MAPHUNZILO ANU A BAIBO KUKHALA PA UBALE WOLIMBA NA YEHOVA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AWA:

  • Cithunzi coonetsa zocitika za m’vidiyo yakuti “Thandizani Maphunzilo Anu a Baibo Kukhala pa Ubale Wolimba na Yehova.” Rose aoneka wankhawa pamene ayankha foni.

    Ni copinga cotani cimene Rose anakumana naco?

  • Cithunzi coonetsa zocitika za m’vidiyo yakuti “Thandizani Maphunzilo Anu a Baibo Kukhala pa Ubale Wolimba na Yehova.” Neeta akukambilana na Rose.

    Kodi Neeta anam’thandiza bwanji Rose?

  • Cithunzi coonetsa zocitika za m’vidiyo yakuti “Thandizani Maphunzilo Anu a Baibo Kukhala pa Ubale Wolimba na Yehova.” Rose asinkhasinkha za mmene Yehova wamuthandizila.

    Kodi Rose anakwanitsa bwanji kugonjetsa copingaco?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani