LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb23 January tsa. 7
  • Konzekelani Palipano Musanadwale Mwadzidzidzi Kapena Kukumana na Ngozi

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Konzekelani Palipano Musanadwale Mwadzidzidzi Kapena Kukumana na Ngozi
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Nkhani Zofanana
  • Mmene Mulungu Amawaonela Magazi
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Yamikilani Mphatso ya Mulungu ya Moyo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
  • Kodi Mumaona Moyo Mmene Mulungu Amauonela?
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
mwb23 January tsa. 7

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Konzekelani Palipano Musanadwale Mwadzidzidzi Kapena Kukumana na Ngozi

N’cifukwa ciyani kukonzekela n’kofunika? Munthu aliyense angadwale mwadzidzidzi kapena kucita ngozi mpaka kugonekedwa m’cipatala. Conco, musanakumane na vuto lamwadzidzidzi, konzekelani bwino lomwe kuti zotelo zikadzacitika, mudzalandile cithandizo cabwino koposa ca mankhwala. Mukacita zimenezi, mudzaonetsa kuti mumalemekeza moyo komanso lamulo la Yehova pa nkhani ya magazi.—Mac. 15:28, 29.

Kodi mungakonzekele bwanji?

  • Pemphelani na kulemba bwino lomwe Khadi Lopatsa Munthu Mphamvu Yosasinthika Yondisankhila Thandizo la Mankhwala (DPA).a Ofalitsa obatizika angapemphe okha khadi la DPA kwa mtumiki wa mabuku, kuphatikizapo khadi la ana awo aang’ono lochedwa Identity Card (ic)

  • Ngati muli na pathupi, pemphani akulu kuti akupatseni fomu yakuti Mfundo Zokhudza Azimayi Apathupi (S-401). Fomu imeneyi idzakuthandizani kusankha bwino cithandizo ca mankhwala pa zovuta zimene zimakhalapo poyembekezela kucila ngakhale pocila kumene

  • Ngati adzafunika kukucitani opaleshoni kapena kukucitani adimiti, dziŵitsani akulu a mumpingo mwanu pasadakhale. Komanso muyenela kufotokozela acipatala kuti, ngati kwabwela mtumiki wa Mboni za Yehova kudzakuonani ayenela kumulola

Kodi akulu angakuthandizeni bwanji? Akulu angakuthandizeni kulemba khadi la DPA. Komabe, sadzakupangilani cisankho pa nkhani za mankhwala kapena kupeleka maganizo awo pa nkhani za munthu mwini. (Aroma 14:12; Agal. 6:5) Mukadziŵitsa akulu a mumpingo mwanu kuti cithandizo ca mankhwala cimene afuna kukupatsani cingafune magazi, iwo mwamsanga adzadziŵitsa Komiti Yolankhula ndi Acipatala (HLC).

Kodi a HLC angakuthandizeni bwanji? Abale a mu HLC amadziŵa bwino mmene angathandizile acipatala komanso a zamalamulo kumvetsa cikhulupililo cathu pa nkhani ya magazi. Iwo angakambe na madokotala za mankhwala kapena njila zina zothandizila odwala m’malo moika magazi. Pakakhala pofunika, angakuthandizeni kupeza dokotala wogwilizanika.

ONELELANI VIDIYO YAKUTI KUPANGA CISANKHO PA CITHANDIZO CA CIPATALA COFUNA MAGAZI, KENAKO YANKHANI FUNSO ILI:

  • Kodi mwaphunzila ciyani mu vidiyo iyi cimene cingakuthandizeni kukonzekela vuto la mwadzidzidzi limene lingabutse nkhani ya magazi?

a Phunzilo 39 m’buku lakuti Kondwelani na Moyo Kwamuyaya lingakuthandizeni popanga zisankho pa nkhani ya cithandizo ca cipatala cimene cingaloŵetsemo magazi.

KODI NDINU WOKONZEKA?

Ngati muyenela kucitidwa opaleshoni kapena kulandila cithandizo ca cipatala cimene cingafune magazi,

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani