LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb23 January tsa. 16
  • Dziikileni Zolinga za pa Nyengo ya Cikumbutso

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Dziikileni Zolinga za pa Nyengo ya Cikumbutso
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Mwalikonzekela Tsiku Lofunika Kwambili M’caka?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
  • Yehova Amadalitsa Kuyesetsa Kwathu Kuti Ticite Cikumbutso
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
  • Pangani Nyengo Ino ya Cikumbutso Kukhala Yosangalatsa
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Cifukwa Cake Timapezeka pa Cikumbutso
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2022
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
mwb23 January tsa. 16

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Dziikileni Zolinga za pa Nyengo ya Cikumbutso

Caka ciliconse, ife anthu a Yehova timayembekezela mwacidwi kusonkhana pamodzi kuti ticite Cikumbutso. Kwa milungu ingapo Cikumbutso cisanacitike komanso pambuyo pake, timaseŵenzetsa mipata yapadela imene timakhala nayo kuti titamande Yehova na kumuyamikila cifukwa ca mphatso ya dipo. (Aef. 1:3, 7) Mwacitsanzo, timayesetsa mmene tingathele kuitanila ena ku Cikumbutso. Ena amakwanitsa kusinthako zinthu zina pa umoyo wawo kuti aciteko upainiya wa maola 30 kapena 50 m’mwezi wa March kapena April. Kodi mungakonde kuwonjezela nthawi imene mumathela mu ulaliki pa nyengo ya Cikumbutso imene ikubwelayi? N’ciyani cingakuthandizeni kucita zimenezi?

Timacita zambili tikakonzekela pasadakhale. (Miy. 21:5) Popeza nyengo ya Cikumbutso ili pafupi, ino ndiyo nthawi yoyamba kukonzekela. Ganizilani mmene mungawonjezele utumiki wanu pa nyengo ya Cikumbutso, komanso zimene muyenela kucita kuti mukwanilitse zolinga zanu. Ndiyeno pemphani Yehova kuti adalitse zoyesayesa zanu.—1 Yoh. 5:14, 15.

Ni njila zina ziti zimene mungawonjezele utumiki wanu pa nyengo ya Cikumbutso?

Zolinga

Zimene niyenela kucita kuti nikwanilitse zolinga zanga

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani