LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb23 March tsa. 3
  • Mmene Tingathandizile Pakagwa Tsoka

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mmene Tingathandizile Pakagwa Tsoka
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Nkhani Zofanana
  • Utumiki Wopeleka Thandizo Pakacitika Ngozi
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila
  • Kupeleka Thandizo kwa Anthu Okhudzidwa na Matsoka
    Mmene Zopeleka Zanu Zimagwilila Nchito
  • Thandizo pa Matsoka a mu 2021—Abale na Alongo Athu Sananyalanyazidwe
    Mmene Zopeleka Zanu Zimagwilila Nchito
  • Kodi Timacita Ciani Pakagwa Tsoka Kuti Tithandize Abale Athu?
    Ndani Amene Akucita Cifunilo Ca Yehova Masiku Ano?
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
mwb23 March tsa. 3

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Mmene Tingathandizile Pakagwa Tsoka

Matsoka a zacilengedwe akuculukila-culukila masiku ano. Tsoka likacitika, nchito yopeleka thandizo iyenela kucitika mwadongosolo komanso iyenela kuyang’anilidwa bwino. Pa cifukwa cimeneci, Bungwe Lolamulila linakonza zakuti pa ofesi ya nthambi iliyonse pakhazikitsidwe Dipatimenti Yoyang’anila Nchito Yopeleka Thandizo Pakagwa Tsoka.

Abale a m’dipatimenti imeneyi akamva kuti ku dela lina kwacitika tsoka la zacilengedwe, mwamsanga amakambilana na akulu a ku delalo kuti adziŵe thandizo limene angapeleke kwa ofalitsa. Ngati zimene zawonongeka n’zambili moti abale a m’delalo sangakwanitse kuthandizana okha-okha, ofesi ya nthambi imasankha abale oyenelela kuti atsogolele pa nchito yopeleka thandizo. Abalewo angapemphe anchito ongodzipeleka kapena angapemphe zinthu zina zofunikila, kapenanso angagule zinthu zofunikila ku dela lomwelo na kuzigaŵila kwa ofalitsa.

Kupeleka thandizo mwa njila imeneyi kuli bwino kusiyana n’kuti abale azingopeleka thandizo pa iwo okha. Kumathandiza kuti nchito imodzi isagwilike kaŵili, pasakhale msokonezo, komanso kuti tisawononge ndalama na zinthu zina zofunikila.

Abale oikidwa na ofesi ya nthambi amadziŵa kuculuka kwa ndalama zimene zikufunika, komanso kuculuka kwa anchito ongodzipeleka amene akufunika pa nchito yopeleka thandizo. Angadziŵanenso na akulu-akulu a m’delalo, amene nthawi zambili amathandiza kufulumizitsa nchito yopeleka thandizo. Conco, anthu sayenela kusonkhetsa ndalama, kutumiza thandizo ku dela limene kwagwa tsoka, kapena kupitako pokhapo ngati auzidwa kucita zimenezi.

Ngakhale n’conco, tsoka likacitika timafuna kupeleka thandizo. (Aheb. 13:16) Timawakonda abale athu! Nanga n’ciyani cimene tingacite? Koposa zonse, tingawapemphelele amene akumana na tsokalo, komanso amene akupeleka thandizo. Tingapelekenso thandizo mwa kucita copeleka ku nchito ya padziko lonse. Motsogoleledwa na Bungwe Lolamulila, maofesi a nthambi ndiwo amadziŵa bwino kumene ndalama zimenezi zingathandize kwambili. Ngati tifuna kukagwila nawo nchito yopeleka thandizo, tingaonetse kuti ndife okonzeka kuthandiza mwa kulemba fomu yakuti Local Design/Construction Volunteer Application (DC-50).

ONELELANI VIDIYO YAKUTI KUSEFUKILA KWA MADZI KOWONONGA KU BRAZIL, KENAKO YANKHANI FUNSO ILI:

Cithunzi coonetsa zocitika za m’vidiyo yakuti “Kusefukila kwa Madzi Kowononga ku Brazil.” Cithunzi coonetsa nyumba na mitengo m’dela limene madzi asefukila.

N’ciyani cimakucititsani cidwi mukaganizila nchito yopeleka thandizo imene Mboni za Yehova zinagwila pamene madzi anasefukila ku Brazil mu 2020?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani