LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb23 May tsa. 3
  • Muzidziona Mmene Yehova Amakuonelani

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Muzidziona Mmene Yehova Amakuonelani
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Nkhani Zofanana
  • Zisankho Zimene Zimaonetsa Kuti Timadalila Yehova
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Muzivomeleza Kuti Pali Zimene Simudziwa
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
  • Muzikhulupirira Kuti Yehova Amakukondani
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
  • Yehova “Amacilitsa Anthu Osweka Mtima”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2024
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
mwb23 May tsa. 3

UMOYO WATHU WACIKHRITU

Muzidziona Mmene Yehova Amakuonelani

“Yehova amasangalala ndi anthu ake.” (Sal. 149:4) Ngakhale kuti ndife opanda ungwilo, Yehova amaona makhalidwe athu abwino komanso zimene tingakwanitse kucita. Komabe, nthawi zina zingativute kudziona mmene Yehova amationela. Tikhoza kumadziona ngati osafunika cifukwa ca mmene anthu ena amacitila nafe zinthu. Mwinanso cifukwa coganizila kwambili zolakwa zathu zakale, tingayambe kukayikila zakuti Yehova amatikondadi. N’ciyani cingatithandize tikayamba kudziona motelo?

Tizikumbukila kuti Yehova amatha kuona zimene ife anthu sitingathe kuona. (1 Sam. 16:7) Izi zitanthauza kuti iye amaona zambili mwa ife kuposa zimene ife eni tingaone. Cokondweletsa n’cakuti Baibo imatithandiza kudziŵa mmene Yehova amationela. Tingadziŵe zimenezi mwa kuŵelenga malemba na nkhani za m’Baibo, zoonetsa kuti Yehova amawakonda kwambili alambili ake.

ONELELANI VIDIYO YAKUTI TSIMIKIZILANI MTIMA WANU KUTI YEHOVA AMAKUKONDANI, KENAKO YANKHANI MAFUNSO AWA:

  • Kodi citsanzo ca tate na mwana wake wothamanga citiphunzitsa ciyani za mmene Yehova amationela?

  • Ngati munthu anacita chimo lalikulu koma anacitapo kanthu kuti akonzenso ubwenzi wake na Yehova, kodi angautsimikizile bwanji mtima wake kuti Mulungu sakumuimba mlandu?—1 Yoh. 3:19, 20

  • Kodi m’bale wa mu vidiyoyi anapindula bwanji ataŵelenga na kusinkhasinkha nkhani za m’Baibo za Davide na Yehosafati?

Nkhani za m’Baibo zimene zimatitsimikizila kuti . . .

Yehova amatikonda mosasamala kanthu za mmene ena amationela

  • Inoki (Gen. 5:24; Aheb. 11:5; Yuda 14, 15)

  • Hana (1 Sam. 1:1–2:11, 18-21, 26)

Ocimwa amene alapa Yehova amawakhululukila na mtima wonse

  • Manase (2 Mbiri 33:1-7, 12, 13)

  • Paulo (1 Tim. 1:12-16)

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani