Sondo, November 9
Usacite mantha.—Dan. 10:19.
Kuti tikhale olimba mtima, kodi tiyenela kucitanji? Makolo athu angatilimbikitse kukhala olimba mtima, koma kulimba mtima kumeneko si coloŵa cimene iwo angangosiyila ana awo. Kukhala olimba mtima kuli ngati kuphunzila luso latsopano. Njila imodzi imene tingakhalile na luso, ni kuyang’anitsitsa zimene wokuphunzitsani amacita, na kutengela citsanzo cake. Mofananamo, timaphunzila kukhala olimba mtima tikamayang’anitsitsa mmene ena amaonetsela khalidweli, na kutengela citsanzo cawo. Monga Danieli, tiyenela kuwadziŵa bwino Mawu a Mulungu. Tiyenela kupanga ubwenzi wathithithi na Yehova mwa kupemphela kwa iye nthawi zonse, na kumuuza mmene tikumvela. Ndipo tizim’dalila, na kukhala otsimikiza kuti adzatithandiza. Ndiyeno cikhulupililo cathu cikayesedwa, tidzakhala olimba mtima Anthu olimba mtima amalemekezedwa na anthu ena. Cina, amakopa anthu oona mtima kuti abwele kwa Yehova. Kukamba zoona, tili na zifukwa zabwino zokhalila olimba mtima. w23.08 2 ¶2; 4 ¶8-9
Mande, November 10
Muzifufuza zinthu zonse.—1 Ates. 5:21.
Liwu la Cigiriki limene analimasulila kuti “muzufufuza,” analigwilitsa nchito pofotokoza mmene anthu amayesela miyala yamtengo wapatali kuti adziŵe ngati ni yeniyeni. Conco, tiyenela kuyesa kapena kuti kutsimikizila zimene timamva kapena kuŵelenga, kuti tidziŵe ngati n’zenizeni. Kudzakhala kofunika ngako kwa ife pamene cisautso cacikulu cikuyandikila. M’malo mokhulupilila m’cimbulimbuli zimene ena amakamba, timagwilitsa nchito luso la kuzindikila kuti tiyelekezele ngati zimene timaŵelenga komanso kumva, n’zogwilizana na zimene Baibo ndiponso gulu la Yehova limakamba. Tikatelo, sitidzapusitsidwa na mauthenga abodza a ziŵanda. (Miy. 14:15; 1 Tim. 4:1) Monga gulu, atumiki a Mulungu adzapulumuka cisautso cacikulu. Koma aliyense payekha amadziŵa kuti cakudza siciimba ng’oma. (Yak. 4:14) Kaya tidzapyola amoyo cisautso cacikulu kapena tidzamwalila cisanafike, tidzalandila mphoto ya moyo wosatha tikakhalabe okhulupilika. Conco, tiyeni tonse tiziganizila kwambili za ciyembekezo cathu cimeneci, ndipo tikhalebe okonzeka tsiku la Yehova. w23.06 13 ¶15-16
Ciŵili, November 11
[Anaulula] cinsinsi cake kwa atumiki ake.—Amosi 3:7.
Sitidziŵa kuti maulosi ena a m’Baibo adzakwanilitsika motani. (Dan. 12:8, 9) Koma kusamvetsa mmene ulosi winawake udzakwanilitsikile sikutanthauza kuti ulosiwo sudzakwanilitsika. Sitipeneka konse kuti Yehova adzatiuza zoyenela kudziŵa pa nthawi yake, monga anacitila kumbuyoko. Coyamba, padzakhala cilengezo ca “bata ndi mtendele.” (1 Ates. 5:3) Kenako, maulamulilo andale adzaukila cipembedzo conyenga na kucifafanizilatu. (Chiv. 17:16, 17) Pambuyo pake, maulamulilowo adzaukila anthu a Mulungu. (Ezek. 38:18, 19) Izi n’zimene zidzabutsa nkhondo yothela ya Aramagedo. (Chiv. 16:14, 16) Ndife otsimikiza kuti zonsezi zatsala pang’ono kucitika. Koma poyembekezela zimenezi, tisaleke kuonetsa ciyamikilo cathu kwa Atate wathu wakumwamba, mwa kuŵelenga maulosi a m’Baibo, komanso kuthandiza ena kucita cimodzimodzi. w23.08 13 ¶19-20