Cisanu, November 7
Azipempha ndi cikhulupililo, asamakayikile ngakhale pangʼono.—Yak. 1:6.
Monga Tate wathu wacikondi, Yehova samakondwela kutiona tikuvutika. (Yes 63:9) Ngakhale n’telo, iye satichinga ku mavuto onse omwe ali ngati mitsinje komanso lawi lamoto. (Yes. 43:2) Komabe, iye analonjeza kuti adzatithandiza ‘tikamadutsa’ m’mavutowo. Ndipo sadzalola kuti mavutowo ativulaze kothelatu. Yehova amatipatsanso mzimu wake woyela womwe ni wamphamvu kuti utithandize kupilila. (Luka 11:13; Afil. 4:13) Conco, tizikhala otsimikiza kuti nthawi zonse tidzakhala na zonse zofunikila kuti tipilile, komanso kukhalabe okhulupilika kwa iye. Yehova amayembekezela kuti tizimudalila. (Aheb. 11:6) Nthawi zina mavuto athu angaoneke osatheka kuwapilila. Tingayambe kukaikila ngati Yehova adzatithandiza. Koma Baibo imatitsimikizila kuti na thandizo la Mulungu ‘tingakwele khoma’ (Sal. 18:29) Conco m’malo molola kuti zikaiko zimenezi zikule mumtima mwathu, tiyenela kupemphela kwa iye mwa cikhulupililo tili na cidalilo cakuti iye adzayankha mapemphelo athu.—Yak. 1:6, 7. w23.11 22 ¶8-9
Ciŵelu, November 8
Kuyaka [kwa cikondi] kuli ngati kuyaka kwa moto. Cikondico ndi lawi la Ya. Madzi ambili sangathe kuzimitsa cikondi, ndipo mitsinje singacikokolole.—Nyimbo 8:6, 7.
Iyi ni njila yabwino kwambili yofotokozela cikondi ceniceni! Mawu amenewa amatsimikizila okwatilana kuti n’zotheka ndithu kukhala na cikondi cosatha. Kuti okwatilana akhale na cikondi cosatha, pali zimene ayenela kucita. Mwacitsanzo, kuti moto usazime timasonkheza nkhuni. Tikaleka kusonkheza, pothela pake moto umazima. Mofananamo, mwamuna na mkazi wake ayenela kusonkheza cikondi cawo kuti cisazime. Nthawi zina, okwatilana angaone kuti cikondi cawo cayamba kuzima, maka-maka akakumana na mavuto azacuma, matenda, kapena akakhala na udindo wolela ana. Kuti “lawi la Ya” lisazime, mwamuna na mkazi wake ayenela kulimbitsa ubale wawo na Yehova. w23.05 20-21 ¶1-3
Sondo, November 9
Usacite mantha.—Dan. 10:19.
Kuti tikhale olimba mtima, kodi tiyenela kucitanji? Makolo athu angatilimbikitse kukhala olimba mtima, koma kulimba mtima kumeneko si coloŵa cimene iwo angangosiyila ana awo. Kukhala olimba mtima kuli ngati kuphunzila luso latsopano. Njila imodzi imene tingakhalile na luso, ni kuyang’anitsitsa zimene wokuphunzitsani amacita, na kutengela citsanzo cake. Mofananamo, timaphunzila kukhala olimba mtima tikamayang’anitsitsa mmene ena amaonetsela khalidweli, na kutengela citsanzo cawo. Monga Danieli, tiyenela kuwadziŵa bwino Mawu a Mulungu. Tiyenela kupanga ubwenzi wathithithi na Yehova mwa kupemphela kwa iye nthawi zonse, na kumuuza mmene tikumvela. Ndipo tizim’dalila, na kukhala otsimikiza kuti adzatithandiza. Ndiyeno cikhulupililo cathu cikayesedwa, tidzakhala olimba mtima Anthu olimba mtima amalemekezedwa na anthu ena. Cina, amakopa anthu oona mtima kuti abwele kwa Yehova. Kukamba zoona, tili na zifukwa zabwino zokhalila olimba mtima. w23.08 2 ¶2; 4 ¶8-9