LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • gf phunzilo 13 tsa. 21
  • Matsenga na Ufiti ni Vinthu Voipa

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Matsenga na Ufiti ni Vinthu Voipa
  • Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Nkhani Zofanana
  • Kudziŵa Zoona pa Nkhani ya Matsenga ndi Ufiti
    Njila ya Kumoyo Wamuyaya—Kodi Mwaipeza?
  • Cokani m’Cipembedzo Conama; Loŵani m’Cipembedzo Coona?
    Njila ya Kumoyo Wamuyaya—Kodi Mwaipeza?
  • Lolani Kuti Yehova Akuthandizeni Kukaniza Mizimu Yoipa
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2019
  • Mutsutseni Mdyelekezi
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
Onaninso Zina
Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
gf phunzilo 13 tsa. 21

Phunzilo 13

Matsenga na Ufiti ni Vinthu Voipa

Satana amafuna kuti muzicita vamatsenga. Anthu ambili amapeleka nsembe ku mizimu ya akufa kuti iziwachinjiliza. Amacita zimenezi cifukwa amaopa mphamvu za mizimu yoipa. Amavala mphete (maling’i) zamatsenga kapena mabango (makhoza). Amamwa kapena kudzola mankhwala amene amaganiza kuti ali na mphamvu zowachinjiliza. Ena amabisa mankhwala mu nyumba kapena kukumbila pansi kuti achinjilize nyumba yawo, kapena kuti kuitsilikila. Palinso ena amene amaseŵenzetsa mankhwala cifukwa amakhulupilila kuti adzawapatsa mwayi pa bizinesi, pamayeso, kapena ofunila mkazi kapena mwamuna.

Njila yabwino kwambili yodzichinjiliza kwa Satana ni kukhala mnzake wa Yehova. Yehova na angelo ake ni amphamvu kwambili kuposa Satana na viŵanda vake. (Yakobo 2:19; Cibvumbulutso 12:9) Yehova ni wokonzekela kuseŵenzetsa mphamvu zake kuti achinjilize anthu amene ni anzake. Ameneŵa ni anthu amene ali okhulupilika kwa iye na mtima wonse.—2 Mbiri 16:9.

Mau a Mulungu amakamba kuti: “Musamacita nyanga kapena kuombeza.” Yehova amazonda zamatsenga, ufiti, kapena kuombeza. Zimenezi amazizonda cifukwa munthu amene amacita zinthu zimenezi amayamba kulamulilidwa na Satana Mdyelekezi.—Levitiko 19:26.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani