LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • th phunzilo 1 tsa. 4
  • Mawu Oyamba Ogwila Mtima

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mawu Oyamba Ogwila Mtima
  • Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Nkhani Zofanana
  • Kumveketsa Phindu ya Nkhani
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
th phunzilo 1 tsa. 4

PHUNZILO 1

Mawu Oyamba Ogwila Mtima

Lemba losagwila mawu

Machitidwe 17:22

ZOFUNIKILA: Mawu anu oyamba afunika kukopa cidwi, kuchula nkhani yanu, komanso kuonetsa mmene nkhaniyo ikuwakhudzila omvela anu.

MOCITILA:

  • Kukopa cidwi. Sankhani funso, mfundo, cocitika, kapena nkhani ya pa nyuzi imene omvela anu angacite nayo cidwi.

    Tumalangizo tothandizila

    Pasadakhale, ganizilani bwino nkhani zimene zingakope cidwi ca omvela anu, ndiyeno konzani mawu oyamba oyenelela.

  • Chulani nkhani yanu. Onetsetsani kuti mawu anu oyamba akumveketsa bwino nkhani yanu kwa omvela, na colinga ca ulaliki wanu.

  • Onetsani cifukwa cake nkhaniyo ni yofunika. Kambani zinthu zothandizadi kwa omvela anu. Afunika kumvetsa bwino-bwino mmene nkhaniyo ingawathandizile.

    Tumalangizo tothandizila

    Pokonzekela nkhani yokakamba mu mpingo, dzifunseni kuti, ‘Kodi abale na alongo mu mpingo mwathu, amakumana na mikhalidwe yotani?’ Ndiyeno konzani mawu oyamba oyenelela mikhalidweyo.

MU ULALIKI

Kuti mupeze mawu oyamba okopa munthu cidwi, yang’anani zimene akucita kapena zili pamalopo. Yambani makambilano anu mwa kumufunsa funso, kapena kukambapo mawu pa zimene mwaonazo.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani