LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • th phunzilo 3 tsa. 6
  • Gwilitsilani Nchito Mafunso

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Gwilitsilani Nchito Mafunso
  • Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Nkhani Zofanana
  • Kumveketsa Phindu ya Nkhani
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Kachulidwe ka Malemba Koyenela
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Yesetsani Kuwafika pa Mtima Omvela
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Mawu Oyamba Ogwila Mtima
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
Onaninso Zina
Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
th phunzilo 3 tsa. 6

PHUNZILO 3

Gwilitsilani Nchito Mafunso

Lemba losagwila mawu

Mateyu 16:13-16

ZOFUNIKILA: Mafunso aluso angakuthandizeni kuwakopa cidwi omvela anu, kulingalila nawo, na kugogomeza mfundo zofunika.

MOCITILA:

  • Kukopa cidwi na kucipitiliza. Funsani mafunso osafuna yankho othandiza munthu kuganiza.

  • Athandizeni kumvetsa nkhaniyo. Athandizeni kutsatila mfundo zanu mwa kuwafunsa mafunso angapo owathandiza kuona mfundo.

  • Gogomezani mfundo zofunika. Funsani funso locititsa cidwi kuti mumveketse lingalilo lofunika. Pambuyo pokambilana kapena kufotokoza mfundo yofunika, kapenanso potsiliza makambilano anu, funsani mafunso obweleza.

    Tumalangizo tothandizila

    Mukaŵelenga lemba, funsani mafunso kuti mugogomeze mfundo yaikulu pa vesi kapena mavesi amene mwaŵelenga.

MU ULALIKI

Pemphani womvela wanu kuti akambepo maganizo ake pa nkhaniyo. Chelani khutu ku zimene akukamba. Onani pamene mungafunsile mafunso aluso komanso mwanzelu.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani