LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • th phunzilo 8 tsa. 11
  • Mafanizo Ophunzitsadi Kanthu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mafanizo Ophunzitsadi Kanthu
  • Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Nkhani Zofanana
  • Seŵenzetsani Mafanizo Pofotokoza Mfundo Zazikulu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
th phunzilo 8 tsa. 11

PHUNZILO 8

Mafanizo Ophunzitsadi Kanthu

Lemba losagwila mawu

Mateyu 13:34, 35

ZOFUNIKILA: Phunzitsani mwaluso pogwilitsila nchito mafanizo osavuta kumva kwa omvela anu, komanso kumveketsa mfundo zofunika.

MOCITILA:

  • Sankhani mafanizo osavuta. Monga mmene Yesu anacitila, gwilitsilani nchito zinthu zing’ono-zing’ono kumveketsa zinthu zikulu-zikulu, komanso zinthu zosavuta kumveketsa zinthu zovuta. Musaphatikizepo mbali zina zosafunikila kweni-kweni zimene zingacolowanitse fanizolo. Onetsetsani kuti fanizo limenelo likugwilizanadi na mfundo imene mufuna kuphunzitsa, kuti musawasokoneze omvela anu.

    Tumalangizo tothandizila

    Khalani wachelu. Muziona mmene zinthu zikuyendela m’dziko, kuŵelenga zofalitsa za gulu, komanso kumvetsela kwa aphunzitsi aluso. Pamene mukutelo, lembani mafanizo amene na imwe mungawaseŵenzetse pofuna kunola luso lanu la kuphunzitsa. Asungeni m’buku kapena m’faelo.

  • Ganizilani omvela anu. Sankhani mafanizo ophatikizapo zinthu zokhudza omvela anu. Koma samalani kuti mafanizo anu asakhale ocititsa manyazi omvela anu, kapena oŵakhumudwitsa.

  • Phunzitsani mfundo zazikulu. Mafanizo anu aziphunzitsa mfundo zazikulu, osati tumbali tocepa. Onetsetsani kuti omvela anu asakakumbukile fanizo cabe, koma maka-maka phunzilo lake.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani