LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lfb phunzilo 20 tsa. 52-tsa. 53 pala. 3
  • Milili 6 Yokonkhapo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Milili 6 Yokonkhapo
  • Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Milili Itatu Yoyambilila
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Mose Ndi Aroni Aonana Ndi Farao
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Mose Anasankha Kulambila Yehova
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Mfumu Yoipa Ilamulila Ku Iguputo
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
Onaninso Zina
Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
lfb phunzilo 20 tsa. 52-tsa. 53 pala. 3
Cigulu ca dzombe

PHUNZILO 20

Milili 6 Yokonkhapo

Mose na Aroni anapita kukauza Farao uthenga wa Mulungu kuti: ‘Ngati sudzalola anthu anga kupita, nidzatumiza tudoyo toyamwa magazi m’dziko lako.’ M’nyumba zonse za Aiguputo, za olemela komanso osauka, munadzala tudoyo utu. Tunali paliponse m’dziko lonse. Koma kudela la Goseni, kumene Aisiraeli anali kukhala, kunalibe tudoyo utu. Kuyambila pa mlili uwu wa namba 4, yonse yokonkhapo inali kugwela Aiguputo cabe. Ndiyeno Farao anapapata kuti: ‘Condelela Yehova kuti acotse tudoyo utu, ndipo nidzalola kuti anthu anu apite.’ Koma pamene Yehova anacotsa tudoyoto, Farao anacinjanso maganizo. Kodi Farao anali wokanga?

Yehova anati: ‘Ngati Farao sadzalola anthu anga kupita, nyama za Aiguputo zonse zidzadwala na kufa.’ M’maŵa mwake, nyama zinayamba kufa. Koma nyama za Aisiraeli sizinafe. Farao anacitabe mwano, ndipo sanawalole kupita.

Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti apitenso kwa Farao kukamwaza phulusa m’mwamba. Phulusalo linasanduka fumbi, cakuti mphepo yonse inali fumbi lokha-lokha kwa Aiguputo onse. Aiguputo onse na nyama zawo anakhala na zilonda zoŵaŵa cifukwa ca fumbi limenelo. Koma Farao anakanilatu kuti Aisiraeli apite.

Milili 4 mpaka 6 ya Aiguputo: tudoyo toyamwa magazi, mlili wa ziweto, vilonda

Yehova anatumanso Mose kwa Farao kukamuuza kuti: ‘Kodi ukali kuletsa kuti anthu anga apite? Mailo kudzagwa cimvula ca matalala.’ Ndipo tsiku lotsatila, Yehova anabweletsa cimvula ca matalala, mabingu, na moto. Cinali cimvula cimene Aiguputo sanacionepo. Cinawononga mitengo na mbewu zonse, koma osati m’dela la Goseni. Farao anati: ‘Pemphani Yehova kuti aletse cimvula ici, kuti mucoke!’ Koma mvula na matalala zitangoleka, Farao anasinthanso maganizo ake.

Lomba Mose anati: ‘Tsopano dzombe lidzadya zomela zilizonse zimene cimvula ca matalala cinasiyako.’ Cigulu ca dzombe cinadya ciliconse cimene cinatsala m’minda na m’mitengo. Farao anacondelela kuti: ‘Pemphani Yehova kuti acotse vidzombe ivi.’ Koma Yehova atacotsa dzombelo, Farao anacitabe mwano.

Yehova anauza Mose kuti: ‘Tambasula dzanja lako ulate kumwamba.’ Pamenepo kumwamba kunacita cimdima candiweyani. Kwa masiku atatu, Aiguputo sanali kuona ciliconse kapena kuonana. Koma kunyumba za Aisiraeli kunalibe mdima.

Milili 7 mpaka 9 ya Aiguputo: matalala, dzombe, mdima

Farao anati kwa Mose: ‘Iwe ndi anthu ako cokani, pitani. Koma musatenge nyama zanu.’ Koma Mose anati: ‘Titenga nyama zathu kuti tikapelekele nsembe kwa Mulungu wathu.’ Farao anakwiya kwambili. Anafuula kuti: ‘Coka pano! Nikadzakuonanso, nidzakupha.’

“Anthu inu mudzaonanso kusiyana pakati pa munthu wolungama ndi woipa ndiponso pakati pa munthu amene akutumikila Mulungu ndi amene sanatumikilepo Mulungu.”—Malaki 3:18

Mafunso: Kodi Yehova anabweletsanso milili iti? Nanga inasiyana bwanji na itatu yoyambilila ija?

Ekisodo 8:20–10:29

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani