LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • th phunzilo 10 tsa. 13
  • Kusintha-sinthako Mawu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kusintha-sinthako Mawu
  • Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Nkhani Zofanana
  • Kukamba Mwaumoyo
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Kukamba Motsimikiza
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Kukambilana Mwacibadwa
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
  • Yesetsani Kuwafika pa Mtima Omvela
    Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
Onaninso Zina
Citani Khama pa Kuŵelenga na Kuphunzitsa
th phunzilo 10 tsa. 13

PHUNZILO 10

Kusintha-sinthako Mawu

Lemba losagwila mawu

Miyambo 8:4, 7

ZOFUNIKILA: Mveketsani bwino malingalilo, ndipo akhudzeni mtima omvela anu posintha-sinthako mphamvu ya mawu, kuwakweza kapena kuwatsitsa, komanso liŵilo lake.

MOCITILA:

  • Muzisintha-sinthako mphamvu ya mawu anu. Wonjezelani mphamvu ya mawu pogogomeza mfundo yaikulu, komanso polimbikitsa omvela anu. Citaninso cimodzi-modzi poŵelenga mawu a ciweluzo a m’Malemba. Cepetsani mphamvu ya mawu pofuna kukopa cidwi, kapena pochula zoopsa, olo zodetsa nkhawa.

    Tumalangizo tothandizila

    Koma osawonjezela mphamvu ya mawu pafupi-pafupi kwambili, cifukwa omvela anu angamve monga mukuwakalipila. Pewaninso kulankhula motentha kwambili pofuna kuti mudziŵike, kapena kuchuka.

  • Muzisiyanitsa kamvekedwe ka mawu anu. Kwezani kamvekedwe ka mawu anu poonetsa kusangalala, ukulu wa cinthu, msenga kaya kuti mtunda. Tsitsani mawu anu poonetsa cisoni kapena nkhawa.

  • Siyanitsani liŵilo la mawu anu. Lankhulani mofulumila kuonetsa cisangalalo. Koma musathamange pofuna kumveketsa mfundo zofunika.

    Tumalangizo tothandizila

    Kuti musadabwitse omvela anu, musamasinthe liŵilo modzidzimutsa. Komanso, musamalankhule mothamanga kwambili cakuti mawu ena samveka bwino-bwino.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani