LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • od masa. 185-192
  • Gawo 1: Zimene ife Akhristu Timakhulupilila

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Gawo 1: Zimene ife Akhristu Timakhulupilila
  • Gulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’ciani?
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Kodi Ufumu Wa Mulungu N’ciani?
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • Muzicita Zinthu Mogwilizana ndi Pemphelo Lacitsanzo—Mbali 1
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
Gulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
od masa. 185-192

MAFUNSO KWA OFUNSILA UBATIZO

Gawo 1: Zimene ife Akhristu Timakhulupilila

Cifukwa cophunzila Baibo na Mboni za Yehova, mwadziŵa coonadi ca m’Baibo. Mosakayika, zimene mwaphunzila zakuthandizani kukhala pa ubale wabwino na Mulungu, ndipo mwakhala na ciyembekezo ca umoyo wa madalitso m’paradaiso pano padziko lapansi mu Ufumu wa Mulungu. Cikhulupililo canu m’Mawu a Mulungu calimba, ndipo poyanjana na mpingo wacikhristu, munayamba kale kulandila madalitso ambili. Mwafika pomvetsetsa mmene Yehova amacitila zinthu na anthu ake lelo lino.—Zek. 8:23.

Pamene mukonzekela za ubatizo lomba, mudzapindula pokambilana na akulu a mpingo ziphunzitso zoyambilila zacikhristu. (Aheb. 6:1-3) Yehova apitilize kudalitsa zoyesa-yesa zanu zofuna kumudziŵa bwino, kuti pothela pake mukalandile mphoto imene analonjeza.—Yoh. 17:3.

1. Kodi n’cifukwa ciani mufuna kubatizika?

2. Kodi Yehova ndani?

• “Yehova ndiye Mulungu woona, kumwamba ndiponso padziko lapansi. Palibenso wina.”—Deut. 4:39.

• “Kuti adziwe kuti inu nokha, dzina lanu ndinu Yehova, ndinu Wam’mwambamwamba pa dziko lonse lapansi.”—Sal. 83:18, BL.

3. N’cifukwa ciani n’kofunika kuti muzilichula dzina la Mulungu?

• “Koma inu muzipemphela motele: ‘Atate wathu wakumwamba, dzina lanu liyeletsedwe.’”—Mat. 6:9.

• “Aliyense amene adzaitana pa dzina la Yehova adzapulumuka.”—Aroma 10:13.

4. Kodi Baibo imachula Yehova na mawu ena ati omufotokoza?

• “Yehova, Mlengi wa malekezelo a dziko lapansi, ndiye Mulungu mpaka kalekale.—Yes. 40:28.

• “Atate wathu wakumwamba.”—Mat. 6:9.

• “Mulungu ndiye cikondi.”—1 Yoh. 4:8.

5. Kodi Yehova Mulungu mungam’patse ciani?

• “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, moyo wako wonse, maganizo ako onse ndi mphamvu zako zonse.”—Maliko 12:30.

• “Yehova Mulungu wako ndi amene uyenela kumulambila, ndipo uyenela kutumikila iye yekha basi.”—Luka 4:8.

6. N’cifukwa ciani mufuna kukhala wokhulupilika kwa Yehova?

• “Mwana wanga, khala wanzelu ndi kukondweletsa mtima wanga, kuti ndimuyankhe amene akunditonza.”—Miy. 27:11.

7. Kodi mumapemphela kwa ndani? Nanga mumapemphela m’dzina la ndani?

• “Ndithudi [ine Yesu] ndikukuuzani, ngati mupempha ciliconse kwa Atate m’dzina langa adzakupatsani.”—Yoh. 16:23.

8. Ni zinthu zina ziti zimene mungapemphelele?

• “Koma inu muzipemphela motele: ‘Atate wathu wakumwamba, dzina lanu liyeletsedwe. Ufumu wanu ubwele. Cifunilo canu cicitike, monga kumwamba, cimodzimodzinso pansi pano. Mutipatse ife lelo cakudya cathu ca lelo. Mutikhululukile zolakwa zathu monga mmene ifenso takhululukila amene atilakwila. Musatilowetse m’mayeselo, koma mutilanditse kwa woipayo.’”—Mat. 6:9-13.

• “Ifetu timamudalila kuti ciliconse cimene tingamupemphe mogwilizana ndi cifunilo cake, amatimvela.”—1 Yoh. 5:14.

9. N’cifukwa ciani nthawi zina Yehova sangamvele mapemphelo a munthu?

• “Adzafuulila Yehova kuti awathandize, koma sadzawayankha. Adzawabisila nkhope yake pa nthawi imeneyo cifukwa ca zoipa zimene anali kucita.”—Mika 3:4.

• “Maso a Yehova ali pa olungama, ndipo makutu ake amamva pembedzelo lawo, koma nkhope ya Yehova imakwiyila anthu ocita zoipa.”—1 Pet. 3:12.

10. Kodi Yesu Khristu ndani?

• “Poyankha, Simoni Petulo ananena kuti: ‘Ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.’”—Mat. 16:16.

11. Kodi Yesu anabwela kudzacita ciani padziko lapansi?

• “Mwana wa munthu sanabwele kudzatumikilidwa, koma kudzatumikila ndi kudzapeleka moyo wake dipo kuwombola anthu ambili.”—Mat. 20:28.

• “Ndiyenela [ine Yesu] kukalengeza uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu kumizinda inanso, cifukwa ndi zimene anandituma kudzacita.”—Luka 4:43.

12. Kodi mungaonetse bwanji kuti mumayamikila nsembe imene Yesu anapeleka?

• “Iye anafelanso onse kuti amene ali moyo asakhale moyo wongodzisangalatsa okha, koma akhale moyo wosangalatsa amene anawafela n’kuukitsidwa.”—2 Akor. 5:15.

13. Kodi Yesu ali na ulamulilo waukulu bwanji?

• “Ulamulilo wonse wapelekedwa kwa ine kumwamba ndi padziko lapansi.”—Mat. 28:18.

• “Mulungu anamukweza n’kumuika pamalo apamwamba. Ndipo anamukomela mtima n’kumupatsa dzina loposa lina lililonse.”—Afil. 2:9.

14. Kodi mukhulupilila kuti Bungwe Lolamulila la Mboni za Yehova ndilo “kapolo wokhulupilika ndi wanzelu” amene Yesu anamusankha?

• “Ndani kwenikweni amene ali kapolo wokhulupilika ndi wanzelu amene mbuye wake anamuika kuti aziyang’anila anchito ake apakhomo, ndi kuwapatsa cakudya pa nthawi yoyenela?”—Mat. 24:45.

15. Kodi mzimu woyela n’ciani?

• “Poyankha mngeloyo anauza Mariya kuti: ‘Mzimu woyela udzafika pa iwe, ndipo mphamvu ya Wam’mwambamwamba idzakuphimba. Pa cifukwa cimenecinso, wodzabadwayo adzachedwa woyela, Mwana wa Mulungu.’”—Luka 1:35.

• “Conco ngati inu, ngakhale kuti ndinu oipa, mumadziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, kuli bwanji Atate wakumwamba! Ndithudi iye adzapeleka mowolowa manja mzimu woyela kwa amene akum’pempha.”—Luka 11:13.

16. Kodi Yehova wakhala akuugwilitsila nchito motani mzimu woyela?

• “Kumwamba kunalengedwa ndi mawu a Yehova, ndipo makamu ake onse analengedwa ndi mpweya wa m’kamwa mwake.”—Sal. 33:6.

• “Koma mzimu woyela ukadzafika pa inu, mudzalandila mphamvu. Pamenepo mudzakhala mboni zanga . . . mpaka kumalekezelo a dziko lapansi.”—Mac. 1:8.

• “Coyamba, mukudziwa kuti ulosi wa m’Malemba sucokela m’maganizo a munthu. Cifukwa ulosi sunayambe wanenedwapo mwa kufuna kwa munthu, koma anthu analankhula mawu ocokela kwa Mulungu motsogoleledwa ndi mzimu woyela.”—2 Pet. 1:20, 21.

17. Kodi Ufumu wa Mulungu n’ciani?

• “Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa ku nthawi zonse. Ufumuwo sudzapelekedwa kwa mtundu wina uliwonse wa anthu, koma udzaphwanya ndi kuthetsa maufumu ena onsewo, ndipo udzakhalapo mpaka kalekale.”—Dan. 2:44.

18. Kodi Ufumu wa Mulungu udzakucitilani zabwino zotani?

• “Iye adzapukuta misozi yonse m’maso mwawo, ndipo imfa sidzakhalaponso. Sipadzakhalanso kulila, kapena kubuula, ngakhale kupweteka. Zakalezo zapita.”—Chiv. 21:4.

19. Nanga mudziŵa bwanji kuti madalitso a Ufumuwo ali pafupi?

• “Ophunzila anafika kwa iye mwamseli ndi kunena kuti: ‘Tiuzeni, kodi zinthu zimenezi zidzacitika liti, ndipo cizindikilo ca kukhalapo kwanu ndi ca mapeto a nthawi ino cidzakhala ciani?’ Poyankha Yesu ananena kuti: ‘. . . Mtundu udzaukilana ndi mtundu wina, ndipo ufumu udzaukilana ndi ufumu wina. Kudzakhala njala ndi zivomezi m’malo osiyanasiyana. Uthenga wabwino uwu wa Ufumu udzalalikidwa padziko lonse lapansi kumene kuli anthu, kuti ukhale umboni ku mitundu yonse, kenako mapeto adzafika.’”—Mat. 24:3, 4, 7, 14.

• “Masiku otsiliza adzakhala nthawi yapadela komanso yovuta. Pakuti anthu adzakhala odzikonda, okonda ndalama, odzimva, odzikweza, onyoza, osamvela makolo, osayamika, osakhulupilika, osakonda acibale awo, osafuna kugwilizana ndi anzawo, onenela anzawo zoipa, osadziletsa, oopsa, osakonda zabwino, aciwembu, osamva za ena, odzitukumula ndiponso onyada, okonda zosangalatsa, m’malo mokonda Mulungu, ndiponso ooneka ngati odzipeleka kwa Mulungu koma amakana kuti mphamvu ya kudzipelekako iwasinthe.”—2 Tim. 3:1-5.

20. Kodi mumaonetsa bwanji kuti Ufumuwo ni wofunika kwambili kwa imwe?

• “Cotelo pitilizani kufunafuna Ufumu coyamba ndi cilungamo cake, ndipo zina zonsezi zidzawonjezedwa kwa inu.”—Mat. 6:33.

• “Yesu anauza ophunzila ake kuti: ‘Ngati munthu akufuna kunditsatila, adzikane yekha ndi kunyamula mtengo wake wozunzikilapo ndipo anditsatile mosalekeza.’”—Mat. 16:24.

21. Kodi Satana ndani? Nanga ziŵanda n’ciani?

• “Inu ndinu ocokela kwa atate wanu Mdyelekezi, . . . Iyeyo ndi wopha anthu ciyambile kupanduka kwake.”—Yoh. 8:44.

• “Cinjokaco cinaponyedwa pansi, njoka yakale ija, iye wochedwa Mdyelekezi ndi Satana, amene akusoceletsa dziko lonse lapansi kumene kuli anthu. Iye anaponyedwa kudziko lapansi, ndipo angelo akenso anaponyedwa naye limodzi.”—Chiv. 12:9.

22. Kodi Satana ananeneza ciani Yehova? Nanga olambila Mulungu amawaneneza zotani?

• “Mkaziyo anayankha njokayo kuti: ‘Zipatso za mitengo yonse ya m’mundamu anatiuza kuti tizidya. Koma zipatso za mtengo umene uli pakati pa munda, Mulungu anati, ‘Musadye zipatso zake ayi, musaukhudze kuti mungafe.”’ Pamenepo njokayo inauza mkaziyo kuti: ‘Kufa simudzafa ayi. Mulungutu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye cipatso ca mtengo umenewu, maso anu adzatseguka ndithu, ndipo mudzafanana ndi Mulungu. Mudzadziwa zabwino ndi zoipa.’”—Gen. 3:2-5.

• “Satana anamuyankha Yehova kuti: ‘Khungu kusinthanitsa ndi khungu. Munthu angalolele kupeleka ciliconse cimene ali naco kuti apulumutse moyo wake.’”—Yobu 2:4.

23. Kodi mungaonetse bwanji kuti zinenezo za Satana n’zabodza?

• “Um’tumikile [Mulungu] ndi mtima wathunthu.”—1 Mbiri 28:9.

• “Mpaka ine kumwalila, sindidzasiya kukhala ndi mtima wosagawanika.”—Yobu 27:5.

24. Kodi n’cifukwa ciani anthu amafa?

• “Ndiye cifukwa cake monga mmene ucimo unalowela m’dziko kudzela mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzela mwa ucimo, imfayo n’kufalikila kwa anthu onse cifukwa onse anacimwa.”—Aroma 5:12.

25. Kodi anthu akufa ali mu mkhalidwe wabwanji?

• “Amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa ciliconse.”—Mlal. 9:5.

26. Kodi pali ciyembekezo canji kwa amene anamwalila?

• “Kudzakhala kuuka kwa olungama ndi osalungama omwe.”—Mac. 24:15.

27. Kodi ni anthu angati amene adzapita kumwamba kukalamulila pamodzi na Yesu?

• “Nditayang’ana, ndinaona Mwanawankhosa ataimilila paphili la Ziyoni. Limodzi naye panali enanso 144,000 olembedwa dzina lake ndi dzina la Atate wake pamphumi pawo.”—Chiv. 14:1.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani