LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp25 na. 1 masa. 4-5
  • Mmene Nkhondo Zimatikhudzila Tonsefe

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mmene Nkhondo Zimatikhudzila Tonsefe
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Nkhondo Zidzatha Liti?—Kodi Baibo Ikutipo Ciyani?
    Nkhani Zina
  • Ndalama Matililiyoni Zawonongedwa pa Nkhondo—Koma Kodi ni Ndalama Zokha Zawonongeka?
    Nkhani Zina
  • Kodi Nkhondo Zidzatha Bwanji?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
  • Nkhondo ya ku Ukraine IIoŵa Caka Caciŵili—Kodi Baibo Ipeleka Ciyembekezo Cotani?
    Nkhani Zina
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
wp25 na. 1 masa. 4-5
Zithunzi: 1. Msilikali akuyenda ndipo kumbuyo kwake kuli kasinja wa nkhondo. 2. Amuna, akazi, ndi ana a mitundu yosiyanasiyana amene anakhudzidwa ndi nkhondo.

Mmene Nkhondo Zimatikhudzila Tonsefe

“Kucokela pa Nkhondo Yaciwili ya Padziko Lonse, nkhondo zaculuka kwambili. Ndipo anthu 2 biliyoni, kutanthauza kuti munthu mmodzi pa anthu 4 alionse padziko lapansi, akukhala kumadela komwe kukucitika nkhondo.”

Anatelo Amina J. Mohammed, waciwili kwa Kalembela Wamkulu wa Bungwe la United Nations pa January 26, 2023.

Mwadzidzidzi, nkhondo ingabuke ngakhale kumalo kumene kuli mtendele. Ngakhale anthu amene akukhala kutali ndi kumene kukucitikila nkhondo amakhudzidwa, cifukwa zimene zikucitika m’dziko lina zimakhudzanso maiko ena. Ndipo pambuyo pakuti nkhondo yatha, mavuto obwela cifukwa ca nkhondo amatenga nthawi yaitali kuti athe. Onani zitsanzo izi:

  • Kacithunzi koonetsa manja awili atanyamula mbale yopanda cakudya.

    Njala. Bungwe Loona za Cakudya Padziko Lonse linati “nkhondo ndiyo cinthu cacikulu cimene cimabweletsa njala padzikoli. Anthu ambili amene akuvutika ndi njala amakhala m’madela amene mukucitika nkhondo.”

  • Kacithunzi koonetsa mzimayi wokhumudwa ataphimba kumaso ndi manja.

    Matenda a maganizo komanso matenda ena. Zikaoneka kuti nkhondo ikhoza kubuka m’dziko linalake, anthu a m’dzikolo amakhala ndi nkhawa yaikulu ndiponso amapanikizika maganizo. Anthu amene akukhala m’madela amene mukucitika nkhondo, amakhala pa ciwopsezo covulazidwa komanso kudwala matenda a maganizo. Ndipo n’zomvetsa cisoni kuti nthawi zambili salandila cithandizo ca mankhwala cimene akufunikila.

  • Kacithunzi koonetsa banja limene lanyamula katundu wawo m’zola zazikulu.

    Anthu amakakamizika kuthawa kwawo. Malinga ndi bungwe la United Nations Loona za Anthu Othawa Kwawo, pofika mu September 2023, padziko lonse lapansi panali anthu oposa 114 miliyoni othawa kwawo. Nkhondo ndiyo cifukwa cacikulu cimene cabweletsa vuto limeneli.

  • Kacithunzi koonetsa banja limene laimilila panja pa nyumba yawo.

    Mavuto a zacuma. Nthawi zambili, nkhondo imabweletsa mavuto a zacuma. Mwacitsanzo, mitengo ya zinthu imakwela. Anthu angavutike ngati boma layamba kutenga ndalama zimene limagwilitsa nchito pa zacipatala komanso pa zamaphunzilo n’kumazigwilitsa nchito pa nkhondo. Komanso pamawonongeka ndalama zambili kuti akonzenso zinthu zimene zinawonongeka cifukwa ca nkhondo.

  • Kacithunzi koonetsa mafuta akucoka m’paipi.

    Kuwonongeka kwa zacilengedwe. Anthu amavutika ngati zinthu zacilengedwe zimene amadalila zawonongedwa. Mwacitsanzo, nkhondo ingacititse kuti madzi, mpweya, ndi nthaka ziwonongeke, ndipo izi zingabweletse matenda osiyanasiyana. Komanso ngakhale patapita zaka zambili pambuyo pa nkhondo, miyoyo ya anthu imakhalabe pa ciwopsezo cifukwa ca mabomba amene anabisidwa m’nthaka.

Conco n’zoonekelatu kuti nkhondo imawononga zinthu komanso ndalama zambili

Maulosi a m’Baibo Okamba za Nkhondo

Baibo inanenelatu kuti nkhondo idzakhala mbali ya “cizindikilo ca mapeto a nthawi ino.” (Mateyo 24:3) Yesu Khristu anati:

  • “Mudzamva phokoso la nkhondo ndi malipoti a nkhondo. . . . Mtundu udzaukilana ndi mtundu wina, ndipo ufumu udzaukilana ndi ufumu wina.”​—Mateyo 24:​6, 7.

  • “Mukadzamva phokoso la nkhondo ndi zipolowe, musadzacite mantha.”​—Luka 21:9.

    Liwu limene analimasulila kuti “zipolowe” lingatanthauze zinthu monga cipwilikiti, kuukila boma, komanso anthu kumenyana pa zifukwa za zandale.

Kuti mudziwe zambili, welengani nkhani yakuti “Kodi Cizindikilo ca ‘Masiku Otsiliza,’ kapena kuti ‘Nthawi ya Mapeto’ N’ciyani?” pa jw.org.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani