LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp25 na. 1 masa. 6-8
  • Kodi Anthu Angakwanitse Kuthetsa Nkhondo?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Anthu Angakwanitse Kuthetsa Nkhondo?
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • KUPITITSA PATSOGOLO ZACUMA
  • KUKAMBILANA ZA MTENDELE
  • KUWONONGA NDI KUCEPETSA ZIDA ZANKHONDO
  • KUPANGA MGWILIZANO WA MAIKO
  • N’cifukwa Ciyani Anthu Akulephela Kukhazikitsa Mtendele?—Kodi Baibo Ikutipo Ciyani?
    Nkhani Zina
  • Kodi Nkhondo Zidzatha Liti?—Kodi Baibo Ikutipo Ciyani?
    Nkhani Zina
  • Kodi Nkhondo Zidzatha Bwanji?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2025
wp25 na. 1 masa. 6-8

Kodi Anthu Angakwanitse Kuthetsa Nkhondo?

Anthu amacita nkhondo pa zifukwa zosiyanasiyana. Anthu ena amamenyana pofuna kuti zinthu zisinthe pa zandale, zacuma, kapena kuti athetse zinthu zopanda cilungamo. Ena amamenyana polimbilana malo komanso zinthu zacilengedwe zamtengo wapatali. Nthawi zambili, nkhondo zimacitika cifukwa cosiyana mitundu kapena zipembedzo. Kodi anthu akhala akucita zotani kuti athetse nkhondo ndi kukhazikitsa mtendele? Kodi zimene akucitazo zingabweletsedi mtendele padziko?

Cithunzi cong’ambika ca ogwila ntchito yomanga nyumba yomwe ili mkati mwa kumangidwa, akukambilana za nchitoyo.

Drazen_/E+ via Getty Images

KUPITITSA PATSOGOLO ZACUMA

Colinga: Kuthandiza anthu kuti akhale ndi umoyo wabwino. Kucita izi kungathandize kuthetsa kapena kucepetsa vuto la kusiyana pa zacuma pakati pa anthu, cifukwa nthawi zina zimenezi n’zomwe zimayambitsa nkhondo.

Colepheletsa: Maboma ayenela kusintha mmene amagwilitsila nchito ndalama zawo. Mwacitsanzo, mu 2022, maboma anagwilitsa nchito madola pafupifupi 34.1 biliyoni pofuna kukhazikitsa mtendele padziko lonse komanso kuusunga. Koma ndalama zimenezi sizinali kukwana ngakhale 1 pelesenti ya ndalama zimene maboma anagwilitsa nchito pa zankhondo m’caka cimeneco.

“Timagwilitsa nchito ndalama zoculuka komanso zinthu zina zambili pothandiza anthu amene akhudzidwa ndi nkhondo, kuposa zimene timagwilitsa nchito pofuna kupewa nkhondo komanso kukhazikitsa mtendele.”​—Anatelo António Guterres, kalembela wamkulu wa bungwe la United Nations.

Zimene Baibo imakamba: Maboma komanso mabungwe angathe kuthandiza anthu osauka, koma sangakwanitse kuthetselatu umphawi.​—Deuteronomo 15:11; Mateyo 26:11.

Cithunzi cong’ambika cokhala ndi manja awili akugwilana canza covomelezana.

KUKAMBILANA ZA MTENDELE

Colinga: Kupewa kapena kuthetsa mikangano mwamtendele mwa kukambilana ndi kucita zinthu zimene zingapindulitse mbali zonse.

Colepheletsa: Gulu limodzi kapena angapo amene akulimbana angakane kukambilana, kulolela, kapena kuvomeleza mgwilizano. Ndipo mapangano a mtendele amaphwanyidwa mosavuta.

“Si nthawi zonse pamene zokambilana zofuna kubweletsa mtendele zimathandiza. Nthawi zina mgwilizano wa mtendele pakati pa magulu awili olimbana ungakhale ndi zopanda cilungamo zambili, zimene zingacititse kuti m’kupita kwa nthawi padzabukenso nkhondo.”​—Raymond F. Smith, American Diplomacy.

Zimene Baibo imakamba: Anthu ayenela ‘kuyesetsa kukhala mwamtendele ndi ena.’ (Salimo 34:14) Koma anthu ambili masiku ano ndi “osakhulupilika, . . . osafuna kugwilizana ndi ena, . . . aciwembu.” (2 Timoteyo 3:​1-4) Makhalidwe ngati amenewa amalepheletsa atsogoleli andale oona mtima kuthetsa mikangano.

Cithunzi cong’ambika ca mfuti yophwanyika.

KUWONONGA NDI KUCEPETSA ZIDA ZANKHONDO

Colinga: Kucepetsa kapena kuwononga zida zankhondo, makamaka za nyukiliya, za mankhwala a poizoni, ndi za tulombo toyambitsa matenda.

Colepheletsa: Nthawi zambili, maiko amakana kucita zimenezi cifukwa coopa kuti angacepe mphamvu kapena angakhale osatetezeka. Koma ngakhale maiko atawononga zida zonse zankhondo, sangathe kuthetsa zinthu zimene zimapangitsa kuti anthu azicita nkhondo.

“Maiko ambili amene analonjeza kuti adzawononga zida zawo zankhondo pambuyo pa caka ca 1991 sanakwanilitse malonjezo awo. Sanakwanilitsenso malonjezo awo akuti adzapewa zinthu zimene zingayambitse nkhondo ndiponso kuti adzacepetsa mikangano pakati pa maiko, n’colinga cakuti pamapeto pake dziko likhale malo amtendele ndi otetezeka.”​—“Securing Our Common Future: An Agenda for Disarmament.”

Zimene Baibo imakamba: Anthu ayenela kusiya zida zawo zankhondo ndi “kusula malupanga awo kuti akhale makasu a pulawo.” (Yesaya 2:4) Koma kuti nkhondo zithe, anthu ayenela kucita zambili cifukwa maganizo aciwawa amacokela mumtima mwa munthu.​—Mateyo 15:19.

Cithunzi cong’ambika ca atsogoleli a mayiko amene akhala pamodzi patebulo. Aliyense akusaina cikalata cimodzi.

KUPANGA MGWILIZANO WA MAIKO

Colinga: Maiko amagwilizana kuti adzathandizana ngati limodzi mwa maikowo laukilidwa ndi adani. Iwo amaganiza kuti adani angaope kuyambitsa nkhondo podziwa kuti akacita zimenezo adzafunika kumenyana ndi asilikali a maiko ambili.

Colepheletsa: Kugwilizana kwa maiko angapo kuti azitetezana dziko lina likaukilidwa sikungabweletse mtendele. Zili conco cifukwa si nthawi zonse pamene maiko amakwanilitsa malonjezo awo. Ndipo nthawi zina sagwilizana za mmene adzathandizilana komanso za nthawi pamene angafunike kutelo.

“Ngakhale kuti mabungwe a League of Nations komanso United Nations. . . anayesetsa kuthandiza maboma kuti apange mgwilizano ndi maboma ena, zimenezi sizinaletse nkhondo kucitika.”​—“Encyclopedia Britannica.”

Zimene Baibo imakamba: N’zoona kuti mu umodzi muli mphamvu. (Mlaliki 4:12) Komabe, maboma a anthu komanso mabungwe sangathe kubweletsa mtendele ndi citetezo ceniceni. Malemba amati: “Musamadalile atsogoleli a anthu. Palibe munthu amene angakupulumutseni. Akamwalila, amabwelela kufumbi. Tsiku limenelo, mapulani awo onse amatha.”​—Salimo 146:​3, 4, Today’s English Version.

Ngakhale kuti maboma ambili akuyesetsa kukhazikitsa mtendele, nkhondo zikupitilizabe kucitika

Kodi padziko pali mtendele woculuka kuposa kale?

Anthu ena amati, masiku ano padziko lapansi pali mtendele woculuka kuposa n’kale lonse. Iwo amati nkhondo za masiku ano sizitenga nthawi yaitali. Amatinso ndi anthu ocepa cabe amene amafa pa nkhondozi poyelekezela ndi amene anafa pa nkhondo zimene zinacitika zaka zambili kumbuyoku. Koma anthu ena sagwilizana ndi zimenezi ndipo amati tiyenela kuganizilanso zinthu zina, osati cabe ciwelengelo ca anthu amene amaphedwa pankhondo.

Ngakhale anthu atakamba zotani, mfundo yosatsutsika ndi yakuti, masiku ano nkhondo zikusautsa anthu ambili padzikoli, amene akukhala m’madela omwe mukucitika nkhondo. Ndipo ngakhale tonsefe timakhudzidwa.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani