29 Mwamuna aliyense amene ndi wansembe azidya nyamayo.+ Ndi yopatulika koposa.+ 30 Koma nyama ya nsembe yamachimo sikuyenera kudyedwa ngati ena mwa magazi ake analowa nawo mʼchihema chokumanako kuti aphimbire machimo mʼmalo oyera.+ Imeneyo muziiwotcha pamoto.’”